Course Content
Kufunika kwa Zisudzo
Chisudzo ndi nkhani yochitika kapena yopeka yomwe imafotokoza zinthu mokhala ngati zikuchitika kumene.
0/2
MITU YONSE MNKHANIYI
0/1
Khoswe Wa Padenga
Kukamba za Bonzo, Goli, Khoswe, Anne ndi Jubeki
0/2
Mudzi Wa Mfumu Tandwe
Kuonongeka kwa zachilengedwe ndi mavuto ena
0/3
CHAMDOTHE NDI ZISUDZO ZINA

 

NUNSU YACHISANU  

Mgezenge akwatira Zikani Mwambo udayamba mwachilendo ndi kuyankhula kwa makolo akuchikazi. Mawu a Gama, bambo a Zikani 

Zikani adamutuma zoti anene kuti iye adasangalala polowa m’banja ndipo ndi amene  adapereka ganizo loti achite shazi. 

Ukwati wa Zikani ndi Mgezenge udalimbitsa ubale womwe udalipo kale. (Adakhala ngati  nyumba yanjerwa yomwe akuyipaka pulasitala wasimenti.) 

Adayamika mkamwini wake Mgezenge kamba ka thandizo lomwe amapereka komanso  kamba ng’ombe ziwiri zomwe adapha patsikuli zomwe nyama yake anthu ankakanika  kuyitsiriza.  

Kumbutso: Akuchimuna sadayankhule popeza padalibepo komanso padalibe yemwe  adawayimirira.  

Zipangizo 

Msemphano: Gama adauza anthu kuti Zikani adamutuma kuti anene kuti iye wakondwa  polowa m’banja komanso adaonjeza kuti Zikani ndi yemwe adapereka ganizo loti achite  mwambo wa shazi chonsecho Zikani sadapereke ganizoli ndipo sadakondwere nkomwe  polowa m’banja.  

MAPHUNZIRO 

  1. Bodza: Gama adauza anthu kuti Zikani adamutuma kuti anene kuti iye wakondwa polowa  m’banja komanso Zikani ndi yemwe adapereka ganizo loti achite mwambo wa. 
  2.  Zinthu zosalongosoka: Pamene Zikani amalowa mbanja ndi Mgezenge monga banja  lachiwiri, akuchikazi padalibe komanso padalibe yemwe adawayimirira mwakuti  sadayankhulepo.  

NUNSU YACHISANU NDI CHIMODZI  

Mkangano kunyumba kwa Mgezenge pambuyo pa ukwati  

Mgezenge akanganana ndi Nagama.  

Mgezenge adauza Nagama kuti akatulutse katundu wake kuchipinda chachikulu chomwe  amagona ndipo akalowe kuchipinda cha alendo kuti apereke danga kwa Zikani.  Nagama adauza Mgezenge kuti iye ndi amene atasamukire kuchipinda chomwe azikagona  ndi Zikani. 

Mokwiya, Nagama adatulutsa katundu wake kuchipinda chachikulu nasiya Mgezenge ndi  Zikani.  

Mgezenge akangana ndi Zikani. 

Atatuluka Nagama zinthu izi zidachitika m’chipindamu:  

Mgezenge adamuyamikira Zikani ndipo adamuuza kuti amuyang’ane; asachite manyazi  popeza ndi mamuna wake.  

Zikani adamuyankha kuti iye ndi bambo wopanda manyazi komanso iye ndi mlamu wake.  Mgezenge adamuuza Zikani kuti panthawiyi sanalinso mlamu wake koma mamuna wake  popeza adasinthidwa. (Chimanga akachigaya sichikhalabe chimanga.) Zikani adatsindika kuti  sankafuna konse.  

Mgezenge adati anthu aakazi amanena zinthu zaukwati ngati sakufuna. Atamufunsira  Nagama sadalole komabe adamukwatira. Zikani adakanitsitsa kuti sankamufuna Mgezenge.  

Pambuyo pake, Nagama adalowanso m’chipindamo nauza Mgezenge ndi Zikani kuti iye  akagona m’chipinda china; Zikani akalowe m’chipinda chachikulu akayale.  Zikani adatsindika kuti Mgezenge sangakhale mamuna wake pazifukwa izi: 

Sanayezetse magazi kuti aone ngati ali bwino kapena ayi. Mchemwali adakhala akudwala  kwa nthawi yayitali koma sanali kudziwa chomwe ankadwala.  

Zimaonetsa kuti Mgezenge ndi Nagama amaopa kuyezetsa magazi.  

Zikani adauza Mgezenge kuti iye adayezetsa ndipo adamupeza ndi kachirombo koyambitsa  Edzi. Apa Mgezenge adamuthamangitsa Zikani m’chipindamo.  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI  

  1. Kudziteteza  

Zikani adatsindika kuti Mgezenge sangakhale mamuna wake pazifukwa izi:  Sanayezetse magazi kuti aone ngati ali bwino kapena ayi 

Iye adayezetsa ndipo adamupeza ndi kachirombo koyambitsa Edzi. (Ili lidali bodza.) 

2. Kusasamala  

Nagama adakhala akudwala kwa nthawi yayitali koma sadaganize zopita kukayezetsa  magazi.  

NUNSU YACHISANU NDI CHIWIRI  

Zikani athawa kunyumba kwa Mgezenge  

Mgezenge podzuka m’mawa, sadamuone ndipo atamufunsa Nagama analinso odabwa  popeza adawasiya awiriwa m’chipinda chachikulu.  

Mgezenge amanena kuti Zikani anakagona kuchipinda limodzi ndi Nagama pamene Nagama  adawasiya awiriwa m’chipinda. Pachifukwachi, Nagama adaganiza Mgezenge adapita  kukamwa mowa usikuwo.  

Adamusakasaka m’zipinda zonse koma sadapezeke.  

Anthuwo adazunguzika popeza Zikani adatuluka pamene zitseko zinali zokhoma.  Nagama ndi Mgezenge adaganiza zokamuyang’ana kwa makolo ake.  

Mgezenge adauza Nagama kuti sangayende asanadye. Pamawu amenewa Nagama adali ndi  maganizo awa:  

Mgezenge akudziwapo kanthu pakusowa kwa Zikani.  

Nkutheka kuti Mgezenge adamupha mtsikanayu ndipo ngati ndi choncho nayenso anali  wokonzeka kuphedwa.  

MAPHUNZIRO  

  1. Kukwiya  

Nagama adakwiya pamene Mgezenge adati ayambe wadya asanapite kukamuyangana  Zikani kwa makolo ake mwakuti adamukalipira Mgezenge kuti ndi mfiti. Kukwiyaku  kudachititsa kuti Mgezenge asinthe maganizo.  

  1. Kusaganiza 

Mgezenge adauza mkazi wake Nagama kuti sangapite kukasaka Zikani asanadye. Izi  Nagama adazitanthauzira kuti mamuna wakeyo amadziwapo kanthu pakuti pamene  adakana zophikazo Mgezenge adalusa namuopseza kuti akadatha kumumenya.  

NUNSU YACHISANU NDI CHITATU  

Mkangano pakati pa makolo a Zikani ndi Mgezenge pa kusowa kwa Zikani Mgezenge ndi Nagama adapita kunyumba kwa makolo a Zikani kuti akamufufuze kumeneko  komabe kunalibe.  

Makolo a Zikani anali odwabwa pakumva za kusowa kwa mwana wawo ndipo adatulutsa  maganizo awa:  

Mgezenge sanayenere kukawafunsa za komwe kunali Zikani popeza anali mkazi wake,  adampatsa ndipo ankakhala naye.  

Ngati adamupha Zikani nkutengako zizimba akadangonena.  

Munthu akakwatira mkazi amakhala kwa mamuna wake osati kwa makolo ake. 

Mgezenge sanayenere kumufunsa Nagama za Zikani pamene Zikaniyo adagona  m’chipinda chimodzi ndi iyeyo.  

Mgezenge adauza makolo a Zikani kuti sakadakamba zoti Zikani adaphedwa pamene  mtembo wake sadawuone.  

Mgezenge ndi apongozi ake onse awiri adagwirizana kuti akanene kupolisi za kusowa kwa  Zikani.  

Zipangizo  

  1. Zifanifani  

Ndikamadya masamba osathira nsinjiro ndimakhala ngati mbuzi yomwe ikudya msipu.  Osamangoti maso tunguluzutunguluzu ngati birimankhwe.  

Iwenso usangokhala ndwii ngati akukuvinira chinamwali.  

  1. Mikuluwiko  

Pamudzi pakhala zitsiru mkamwini asamakulirepo mwendo: Mgezenge anayenera kupereka  ulemu kwa apongozi pamene anawapeza pakhomo pawo posatengera kuti anali amphawiNkhuyu zodya mwana zidapota akulu: Chilichonse chomwe chidachitika pa Zikani  chidakhudzanso makolo ake.  

  1. Mvekero  

Tunguluzutunguluzu: kuyang’ana uku ndi uku  

Ndwii: kukhala osayankhula koma kumangoyang’anitsitsa  

4) Msemphano 

Mwana akalirira fupa, muninkhe: likamuthyola dzino, ndi zake zimenezo: Zikani  sadawumirire kukwatiwa ndi Mgezenge; adamuwumiriza ndi makolo ake mwakuti pamene  adasowa Mgezenege ndi makolo ake anayenera kumusakasaka.  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI  

1) Kupanda ulemu  

Mgezenge adafika ndi ukali pakhomo pa apongozi ake komanso ankayankhula ali chilili. 

2) Kusokonezeka  

Nagama ankakanika kuyankha mafunso atapita kwa makolo ake popeza adasokonekera  ndi kusowa kwa mchemwali wake Zikani.  

error: Content is protected !!
Scroll to Top