Course Content
Kufunika kwa Zisudzo
Chisudzo ndi nkhani yochitika kapena yopeka yomwe imafotokoza zinthu mokhala ngati zikuchitika kumene.
0/2
MITU YONSE MNKHANIYI
0/1
Khoswe Wa Padenga
Kukamba za Bonzo, Goli, Khoswe, Anne ndi Jubeki
0/2
Mudzi Wa Mfumu Tandwe
Kuonongeka kwa zachilengedwe ndi mavuto ena
0/3
CHAMDOTHE NDI ZISUDZO ZINA

NUNSU YACHISANU NDI CHINAYI  

Anthu akhudza maliro a Zikani ngakhale iye sadamwalire  

Ngakhale anthu sadaone mtembo wa Zikani, adakhulupirira kuti adamwalira.  Umboni woti Zikani adamwalira  

Panalibe umboni weniweni woti Zikani adamwalira. Anthu adakhulupirira izi:  Atsikana awiri omwe ankakhala m’nyumba yomwe alonda ankhalango adayisiya ndipo  zinkamveka kuti adathawa mabanja awo ndipo m’modzi mwa iwo ankati ndi Zikani,  adaphedwa ndi afisi ndipo kunali kovuta kuzindikira nkhope zawo. Matupi awo adalibe  ziwalo zina.  

Umboni woti atsikana omwe ankakhala m’nyumba yam’nkhalango adamwalira  Patapita masiku angapo afisi adavuta m’midzi yoyandikana ndi nkhalangoyo.  Sabata idatha atsikanawo asadaonekenso.  

Anthu adamva fungo loyipa kuchokera kunkhalango ndipo atalowa m’nkhalangomo  adapeza matupi awiri ataonongeka kwambiri. Matupiwo adali a atsikana.  

Umboni woti m’modzi wa atsikanawo anali Zikani  

Mphekesera zinamveka kuti atsikanawa ankapita ku sukulu zosiyanasiyana nkumakauza  atsikana anzawo za ufulu wa maphunziro a atsikana. Izi ndi zomwe Zikani adauzanso  makolo ake pamene ankamuuza zoti akwatiwe ndi mlamu wake Mgezenge.  M’modzi mwa iwo ankafanana ndi Zikani.  

Atsikanawo atafunsidwa mayina awo, adakana kutchula powopa kuti angakawabwezere  kumabanja komwe adathawa. Panthawiyi nkuti Zikani atathawa kubanja kwa Mgezenge.  

Kumbutso:  

Malingana ndi wotsogolera mwambo wamaliro a Zikani zidali zokayikitsa ngati m’modzi  mwa atsikana omwe adaphedwa ndi afisiwo anali Zikani popeza nkhope zawo zidadyedwa  kotero kuti kunali kovuta kuwazindikira kuti adali yani ngakhale panali madiresi omwe anthu  ankati anali a atsikanawo.  

Anthu adakhulupirira kuti afisiwo adali a munthu ndipo kuti mwiniyo anali Mgezenge. 

Mwa mwambo wake, popeza mtembo wa Zikani panalibe, amuna angapo adapita kumanda  n’kukakwirira thunthu lanthochi m’dzenje lamanda poopa kuti mzimu wa malemu Zikani  ungawasautse m’mudzimo.  

Amfumu adachitira umboni kuti Zikani anali mwana wamakhalidwe abwino.  

Zikani atulukira pamaliro ake  

Adatulukira pamodzi ndi mzake.  

Mgezenge, Abiti ndi a Gama adamuona.  

Mgezenge adachita mantha poyesa ndi mzukwa.  

A Gama, bambo ake, adalimba mtima n’kumuyandikira komanso kumugwira kenako  n’kuthawa.  

Amfumu adamuponyera dothi kuti awone ngati ndi mzukwa kapena munthu weniweni  popeza mzukwa umazimirira akawuponyera dothi. Zikani sadazimirire.  

Atate ake, a Gama, adafuna kudziwa kuti zidatheka bwanji munthu wakufa n’kudzukanso.  Iye adatsindika kuti iye simalemu ndipo pamoyo wake sadafepo; ndi mwana wa Mulungu  yekha basi yemwe adadzukapo.  

Mgezenge adakuwa kuti mkazi wake sadafe; adali ndi moyo koma Zikani adakanitsitsa kuti  sadali mkazi wake. Iye adasowa chifukwa ankamuthawa Mgezengeyo.  

Adanena mosaopa kuti Mgezenge ndi chidyamakanda, munthu woyipa komanso wopusa.  (Adali ngati nkhuku yodzimwera mazira ake omwe popeza adamulera yekha Zikani kenako  n’kumafunanso akhale mkazi wake.)  

Mawu a Zikani pa nkhani ya atsikana omwe adaphedwa ndi afisi  

Matupi omwe adapezekawo anali a atsikana anzake omwe adathawa kumabanja  okakamizidwa. Nawonso adathawa mwambo wa shazi ndi amuna adyera monga Mgezenge.  Zovala zake zidapezeka ndi atsikanawo popeza sadapeze mpata wotenga zovala zawo  pamene ankathawa kumabanjako mwakuti Zikaniyo ndiye adawabwereka zake.  Atsikanawa, Sibongile ndi Malita, adaphedwa ndi afisi atangochapa zovala zawo. Iye ndi  mnzake, Chisomo, adapulumuka popeza adathawira kutali atangomva phokoso la afisiwo.  Iwo adathawira kwa mayi wina wopemphera yemwe adawalimbikitsa kupempherera mizimu  ya anzawo awiriwo.  

Atamva kuti anthu akulira maliro ake, iye adabwera mwansanga kuti anthu adziwe zoti iye  adakali moyo.  

Tsoka la mnzake wa Zikani (Chisomo Mwayikale)  

Makolo ake ankakongola ndalama kwa munthu wina wolemera dzina lake Mwenekuchanya.  Atalephera kubweza ndalamazo, makolowo adagwirizana ndi Mwenekuchanya kuti Chisomo  akhale mkazi wake wachinayi ngakhale anali wachichepere kwambiri (ali ndi zaka zisanu). 

Makolowo adakamupereka kwa njondayi (Mwenekuchanya) ali sitandade 7. Mwambowu  umenewu umatchedwa “Kupimbila” kapena “Kupawila”.  

Iye adathawa tsiku lomwelo ndipo adakwera basi ngakhale adalibe ndalama.  Atawafotokozera anthu zomwe zidamchitikira, adamuthandiza. Iye ankati akupita kwa  amalume ake kuboma ngakhale kuti komwe ankalowera sankakudziwa. Mwamwayi  adakumana ndi Zikani atangotsika basi ndipo adayamba kukhalira limodzi.  

Mawu a amfumu atamva nkhani ya Chisomo  

Atamva izi adati adachita manyazi nati sadayenere kuloleza ukwati wa Zikani kuti uchitike.  Adauza anthu onse kuti miyambo yina n’kutheka idali yabwino pachiyambi koma anthu  adayisokoneza. N’kuthekanso makolo ena anali adyera. Miyambo ina mwina idayamba  makolo atasauka.  

Adalamula kuti miyambo monga hlazi ndi chimeta masisi itheretu m’mudzimo.  

Mgezenge ayambitsa chisokonezo.  

Iye adatsindika zomutengabe Zikani kukhala mkazi wake ngakhale zikadavuta motani.  Adati anthu ena adadya ndalama zake choncho adayenera kubweza.  

Mgezenge adati miyamboyo ikamatha, iye akhala atamutenga mkazi wake, Zikani. Kupanda  kutero akadavulaza munthu wina. Iye adaopseza kuti kusintha miyambo kusayambire pa  iyeyo.  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI  

  1. a) Ana adazunzika kamba ka umphawi wamakolo  

Makolo a Chisomo adamukwatitsa ali wachipere kwa mkulu yemwe adakanika  kumubwezera ndalama zake atakongola. Chisomo adathawira kunyumba ina yomwe  adayisiya alonda ankhalango. M’nyumba m’menemu ndi momwe anzawo ena awiri  adaphedwa ndi fisi.  

Zikani adathawa ku banja lokakamizidwa ndipo ankakhala m’nyumba ina yomwe  adayisiya alonda ankhalango.  

  1. Chisoni  

Anthu omwe adamva nkhani ya Zikani adamuthandiza kuti ulendo wake upitirire.  c. Chikondi  

Zikani adawabwereka zovala atsikana omwe adaphedwa ndi afisi popeza pobwera  kwawo sadatenge zovala.  

  1. Nkhanza  

Makolo a Zikani ndi Chisomo adakwatiwitsa ana awo mowakakamiza asadafike  pamsinkhu woyenera kutero.  

  1. Kudziteteza 

Zikani ndi Chisomo adathawa ku mabanja okakamizidwa komanso adathawa afisi olusa  napita kwa mayi wina komwe ankapempherera mizimu ya anzawo awiri amene  adaphedwa ndi afisiwo.  

  1. Kulongosola/Kuwongola zinthu  

Amfumu adathetsa mwambo wa shazi/ mbirigha/ isakulwa/ chimeta masisi  g. Kuipa mtima/Kusamva  

Mgezenge adalimbikira zoti amutengabe Zikani ngati mkazi chonsecho amfumu  adalengeza kuti adathetsa mchitidwe wa shazi m’mudzi mwawomo.  

NUNSU YAKHUMI  

Sukulu ipindulira Zikani, Funsani ndi Chisomo 

Anthu atatuwa adaphunzira ndipo adali pantchito. Chisomo ankagwira ntchito limodzi  ndi Zikani mbungwe la “Mtetezi wa Mwana” lomwe adayambitsa Zikani. Macheza a Chisomo ndi Funsani 

Chisomo adafika kunyumba kwa Funsani ndi Zikani kuti akapereke lipoti lantchito  yomwe adakagwira ku esiteti ina komwe zimamveka kuti mwini wake ankagwiritsa  ntchito ana aangono. 

Chisomo adasankha kupatsidwa madzi m’malo mwa chakumwa chilichonse ndipo adati:

Zakumwa zisamakhale ndi shuga wambiri komanso zothiramo zosadziwika.

Agogo ake adawadula mwendo ndipo matenda ashuga ndiwo adali gwero.

Funsani adauza Chisomo kuti kusankha madzi isakhale njira yopulumutsira makobili  pozemba zakudya zabwino popeza atsikana makobili amathera mmutu. 

Macheza a Chisomo, Zikani ndi Funsani 

Chisomo adauza Zikani kuti adabwera kudzamuuza m’mene adayendera ku esiteti  komwe kudamveka kuti mwini wake akugwiritsa ntchito ana aangono. 

Adakumbutsana zakale ndipo adakamba zotsatirazi: 

Akadapanda kuchita khama bwenzi panthawiyi atakalamba; sakadaphunzira monga  adachitira panthawiyi. 

Sukulu ndi yabwino popeza idathandiza kuti ayambitse bungwe la “Mtetezi wa Mwana”. Matenanti a ku esiteti ina adakadandaula ku ofesi ya Zikani ndi Chisomo. M’modzi mwa  matenantiwo adali ndi ana asanu ndi awiri. Onsewo amagwira ntchito pa esiteti  pomwepo. Anawo ankavutika popeza ankagwira ntchito zolemetsa komanso sankapita  kusukulu. 

Funsani adakumbukira m’mene ankagwirira ntchito kugolosale kwa a Mgezenge:  amagwira ntchito n’kumalipidwa zovala zakale. 

Zikani adagwirizana ndi Funsani kuti Zikani adachita bwino kuthawa kwa a Mgezenge  popeza a Mgezenge adali kudwaladwala mwakuti adaonda kwambiri ndipo Nagama adamwalira. Chuma chonse chidatha: ng’ombe zidathera malipiro asing’anga, golosale  adatseka.

Zikani adalakalaka akadathandiza makolo ake koma panthawiyi anali atamwalira. Zotumphuka pa macheza a Zikani, Funsani ndi Chisomo kunyumba kwa Funsani ndi  Zikani 

Chilonda chimavuta kupola ndi matenda a shuga. 

Nsima yamgayiwa ndi yabwino popeza imakhala ndi madeya ofunika m’thupi komanso  ili ndi sitalichi ndi faiba wambiri. Nsimayi imathandiza kupewa matenda amtima ndi  khansa.  

Patapita nthawi Zikani adakwatiwa ndi Funsani  

Zikani adayambitsa bungwe la “Mtetezi wa Mwana” ndipo anali bwana wamkulu.  Chisomo adali mthandizi wake.  

Azungu a mishoni ndi omwe adalipirira sukulu Funsani mpaka ku yunivesite ndipo  adamupezeranso ntchito. Azunguwa adapita kumwambo wolandira madigiri monga  makolo a Funsani. M’modzi mwa azungu amishoniwa anali Bambo Alfred.  

Eni esiteti akalemba bambo ntchito, ndiye kuti banja lonse limagwira ntchito yomweyo.  Eni esiteti anali oyipa pazifukwa izi:  

Ndi iwo okha amene amagula fodya wamatenanti.  

Amagula fodya wamatenanti pa mtengo wozizira.  

Amalamula mtengo wogulira fodya wamatenanti awo.  

Amawapatsa matenanti zakudya zosakwanira.  

Makolo a Zikani komanso Funsani anali atamwalira panthawiyi.  

Zikani ndi mamuna wake Funsani ankacheza moserewulana.  

Zikani adanena moserewula za ntchito yakale ya Funsani: “Ikakhala golosale yako ija  muli akangaude okhaokha.”  

Funsani adanena moserewula za ukwati wa Zikani ndi Mgezenge: “Amuna ako aja anali  wovuta kwambiri.”  

Zipangizo  

  1. Zining’a  

o Fisi asanathyole khola: asanagonane  

o Anatsikira kulichete: Anamwalira  

o Ali mafupa okhaokha: Adaonda kwambiri.  

o Ndi bwenzi wa mphasa: Akudwaladwala.  

o Onse anatsogola: Anamwalira.  

o Pamtengo wozizira: Pamtengo wotsika  

o Makobiri akuthera m’mutu: Makobiri akuthera kukonza tsitsi.  

o Tawonjola ana ambiri: Tapulumutsa ana ambiri.  

  1. Chifanifani  

Ndinkakhalira mphanthi ngati nsikidzi.  

Ndinkakhala movutika kwambiri.  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI 

1) Chikondi  

Azungu amishoni adamutenga Funsani makolo ake atamwalira n’kumakhala naye ndipo  adamulipirira sukulu mpaka ku yunivesite. Atatsiriza ku yunivesite, adamupezera ntchito. 

2) Nkhanza  

A Mgezenge ankamugwiritsa ntchito Funsani ku golosale koma ankamulipira zovala  zokutha.  

Eni esiteti ankawachitira nkhanza zosiyanasiyana matenanti awo. 

3) Kukonda/Kusamala ntchito  

Zikani adafuna kumva kaye m’mene Chisomo adayendera ku esiteti komwe kudamveka kuti  mwini wake akugwiritsa ntchito ana aang’ono. Adachita zimenezi atangofika kuchokera  kuntchito, asadapume ngakhale mwamuna wake Funsani adamuuza kuti ayambe wapuma. 

4) Kudziwa zinthu  

Chisomo adachenjeza Funsani pa nkhani ya zakumwa zashuga wambiri komanso zothiramo  zosadziwika. Adamufotokozeranso za matenda a shuga ndi momwe adachititsira kuti agogo  ake adulidwe mwendo. Mtsikanayu adafotokozanso za kufunika kwa nsima yamgayiwa.  

NUNSU YAKHUMI NDI CHIMODZI  

Zikani ndi Chisomo ku esiteti  

Adafika pakhomo pa a Kamwendo atavala zitenje ndi mipango ndipo adalonjeredwa. Bambo  Kamwendo anali tenanti.  

Ataona mwana wina wa a Kamwendo atasenza mtolo wankhuni waukulu kuposa msinkhu  wake, Zikani adafunsa modabwa popeza mnyamatayo anayenera kukhala ali kusukulu  panthawi monga imeneyi.  

Zikani adawafunsa chiwerengero cha ana omwe adali nawo komanso momwe amaliwonera  tsogolo lawo ndipo a Kamwendo adayankha izi:  

Ali ndi ana asanu ndi awiri.  

Mwana amene adadutsa ndi mtolo anali wachinayi.  

Ana ena anali kuganyu yopalira.  

Mwana wawo wamkazi adapita kutauni kukagulitsa masamba.  

Ana awiri aang’ono adaperekeza mayi awo kuchigayo.  

Anawo sakadamapita kusukulu tsiku lililonse popeza sakadapezako chakudya. 

Amawaphunzitsa anawo momwe angadzakhalire akadzakula; amawaphunzitsa ntchito.  

Zomwe Zikani adaunikira a Kamwendo koma sadazimvetse 

Ntchito zomwe ana aangono amagwira pakhomo zizifanana ndi msinkhu wawo. Kholo logwiritsa ana ntchito zoipa litha kumangidwa. 

Dziko lidasainira mgwirizano pa 17 June 1999 wa “Mitundu ya Ntchito Zoyipitsitsa kwa  ana” “Worst Forms of Child Labour Convention” womwe gawo 3 limakamba za ntchito  zomwe zingathe kuononga moyo wamwana.

Zimaonetsa kuti a Kamwendo sakulera bwino ana: samawapititsa kusukulu nthawi zonse,  amawagwiritsa ntchito zomwe zikadatha kuononga moyo wawo. Chitsanzo chinali cha  mwana amene adadutsa ndi mtolo wankhuni yemwe amaoneka kuti adakakamizidwa kutero. 

A Kamwendo adawathamangitsa Zikani ndi Chisomo ponena kuti sangawalamulire za ana  awo poti iwo adalibe ana komanso sankadziwa chilichonse chokhudza mwana.  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI 

  1. Kusazindikira 

A Kamwendo ankagwiritsa ntchito ana awo mobzola msinkhu wawo komanso  ankawajombetsa kusukulu nthawi zambiri, kotero samadziwa kufunika kwa sukulu. 2. Kusaphunzitsika 

A Kamwendo sadamvetse kuti kugwiritsa ana awo ntchito mopitirira mulingo ndi  kuwachitira nkhanza. M’malo mwake iwo adatanthauzira kuti Zikani ankawauza kuti  anawo asamagwire ntchito mwakuti adamulalatira namuopseza kuti achoke pakhomopo  asadamukhwiyitsire agalu. 

  1. Kuteteza 

Zikani adayambitsa bungwe la “Mtetezi wa Mwana” kuti awonjole/apulumutse ana  kumavuto a kugwiritsidwa ntchito zosagwirizana ndi msinkhu wawo komanso kusapita  kusukulu. 

NUNSU YAKHUMI NDI CHIWIRI  

Mgezenge kunyumba kwa Zikani ndi Funsani 

Adafika akudziyankhulira zinthu izi: 

Abale ake onse adamwalira. 

Adali wolemera koma zinthu zonse (mbuzi, ng’ombe, sitolo, nkhuku ndi nkhunda)  zidatha. 

Pa esiteti yake boma lidamanga sukulu ndipo ndalama zachipukutamisozi zidatha  kalekale. 

Msewu womwe udadutsa mmunda mwa apongozi ake umalunjika kusukulu. Anthu akamuona, ankamutcha wamisala kapenanso sing’anga. 

Adaganiza zopempha malo ogona panyumba ina yomwe sankadziwa kuti inali ya  Funsani ndi Zikani.  

Adachita odi ndipo Chisomo Mwayikale ndiye adamulonjera.  

Adamuuza Chisomo kuti akawauze eni nyumba kuti iye ankafuna malo ogona; tsiku  lotsatiralo azipita.  

Chisomo adauza Mgezenge kuti mnzakeyo adavomera kuti amusunga ndipo akagona  kunyumba yogona anyamata. Adamutengera Mgezenge kunyumba yayikulu kuti  akamuone. 

Funsani adawazindikira a Mgezenge ndipo Chisomo adawadziwanso koma iwo  sadawazindikire.  

Zikani adawadziwitsa a Mgezenge kuti iyeyo ndi Zikani ndipo mamuna wake ndi  Funsani. 

Mgezenge adapepesa.  

Funsani ndi Zikani adakhululukira Mgezenge pa zonse zomwe adawachitira.  Zikani adauza wantchito wake kuti awasamalire a Mgezenge ku chipinda cha alendo.  Chisomo adatsanzika n’kumapita kwawo.  

Zipangizo Zining’a  

  1. a) Onse kutha psiti: Onse kumwalira  
  2. b) Ndiwone msana wanjira: Ndizipita  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI  

  1. Kunong’oneza bondo  

Mgezenge adadziyankhulira yekhayekha modandaula kuti kunja kuyanja lichero. Iye  adali ndi chuma koma chidatha chonse. Abale ake onse adamwalira ndipo anthu  akamuona akumunena kuti ndi wamisala komanso sing’anga.  

  1. Chuma ndi mchira wakhoswe sukhalira kupululuka  

Mgezenge adali ndi chuma chambiri ndipo ankachitira anthu nkhanza. Adagwiritsa  ntchito chuma chake kuti akwatire mlamu wake Zikani. Chuma chonsecho chidatha  ndipo adasauka mwakuti anthu akamuona ankamuyesa wamisala.  

  1. Kukhululuka  

Zikani ndi mwamuna wake Funsani adamukhulukira Mgezenge ngakhale adawachitira  zoyipa. Atafika pakhomo pawo atasaukiratu komanso atadwalika kwambiri n’kupempha  malo ogona, anthu awiriwa adamusamala Mgezenge.  

  1. Kusayiwala  

Funsani adakumbukira zonse zomwe Mgezenge adachitira Zikani ndi iye yemwe. Iye  adati Mgezenge adali katswiri pogwiritsa ana ntchito yakalavula gaga, iye adali kapolo  wake, adali chidyamakanda ndipo Zikani adatsala pang’ono kufa kamba ka iye.  

NUNSU YAKHUMI NDI CHITATU  

Mgezenge adzikhweza pakati pa usiku  

Wantchito wa Funsani ndi Zikani adayimbira foni Funsani kuti anamva phokoso  losonyeza kuti munthu ankaphupha mobanika ndipo atathamangira m’chipinda momwe  adagona Mgezenge, adapeza atadzimangirira ndi chingwe choyanikapo zovala.  

Funsani ndi wantchito adathandizana kuswa chitseko ndipo adampeza Mgezenge asadafe.  Adayitanitsa makiyi a galimoto kuti amutengere kuchipatala. 

Chipangizo Mkuluwiko  

Chifundo chidapha nkhwali: Chisoni chomwe Funsani ndi Zikani adachitira Mgezenge  pompatsa malo ogona chikadawabweretsera mavuto pamene Mgezenge adadzimangirira.  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI  

Kudziweruza: Mgezenge adadzimangirira kuti afe popeza kudali kovuta kuti akhale  m’nyumba mwa Funsani ndi Zikani poganzira nkhanza zomwe adawachitira pamene iye  adali ndi chuma.  

Moyo ndi wozungulira: Mgezenge adakapempha chithandizo kunyumba kwa Funsani pamene m’mbuyomo Mgezenge ndi amene adalemba ntchito Funsani yogulitsa m’golosale  mwake.  

MAKHALIDWE A BAMBO MGEZENGE 

1) Wandeu 

Akumuponyera chibakera Nagama chifukwa choti sakugwirizana ndi maganizo oti  akahale awiri 

Akwenya Funsani pa khosi chifukwa chopezeka ndi cholembera mu thumba lake. Iwo  amaganiza kuti waba mu golosale yawo yomwe iye akuwagulitsira ngati wantcito 2) Wosaganizira ena (wosalabadira mavuto a anzake) 

Mayamiko awabweretsera nkhuni ndipo ayembezera kuti apatsidwe ndalama kuti akagule  sopo yochapira zovale kuti azipita bwino ku sukulu. A Mgezenge aumuuza kuti akathana  ndi abambo ake osamupatsa kena kalikonse 

3) Waukali  

Akalipira Nagama pa china chilichonse chomwe atalakwitse 

Tsiku lina pochapa, Nagama apempha Zikani kuti awathandize kuchapa. Koma  amulangiza kuti asawauze a Mgezenge kuopa kukalipiridwa 

4) Wachipongwe  

Amusiyitsa ntchito Funsani chifukwa chotseka shopu. Iye anatseka shopu chifukwa  anapita ku chipatakla atadwala malungo 

5) Wopanda ulemu 

Apita kwa apongozi ake (Abiti ndi Gama) nawawuza kuti abwera kudzangosiya mwana  wawo. Akupanga izi asanakhale ndi pansi. 

MAKHALIDWE A ZIKANI 

  1. Wozindikira  

Awuza a Mgezenge kuti kuti sangakhale mkazi wawo popeza ndi mlamu wawo Awuza a Mgezenge kuti sangagonane asanakeyedzetse magazi 

  1. Wolimba mtima 

Awuza makolo ake kuti iyeyo sangakhale mkazi wa Mgezenge

Awuza a Mgezenge kuti iye ndi mlamu wawo osati mkazi wawo  

  1. Wachisoni  

Amalira pa ukwati chifukwa chosafuna kuti akhale mkazi wa Mgezenge d. Wa chikondi  

Ayambitsa kalabu yotchedwa Mtetezi wa Mwana ndi cholinga choteteza ana omwe  akuponderezedwa mu ma esiteti ndi malo ena 

  1. Wokhululuka  

Anakhululukira a Mgezenge pa nkhanza zomwe ankanamuchitira pamene anapita  kunyumba kwawo pofuna malo ogona 

MFUNDO ZIKULUZIKULU 

  1. Miyambo 

Mwambo wopereka ma digiri kwa ophunzira 

Mwambo wa ukwati wa Zikani ndi Bambo Mgezenge 

Mwambo wa maliro a Zikani  

Mwambo wa chikhalidwe chamakolo: kupereka Zikani kwa mlamu wake, Mgezenge,  mbiriya 

  1. Zikhulupiriro  

Mulungu: Zikani anati makolo ake anali ku mwamba ndi mulungu. Mzimayi  wopemphera adamutenga Zikani pomwe anathawa a Mgezenge 

Ufiti: Abiti ndi Gama amakhulupirira kuti a Mgezenge amupha Zikani kuti alemere. Mizimu: pa mwambo wa maliro anati, mu dzenje akatayamo thunthu la nthochi ndi  kulikwirira kuopa kuti azimu angaphe munthu wina mu mudzimo. Zikani anati mizimu  wa Sibongire ndi Malita (atsikana odyedwa ndi afisi kunkhalango) ukhala mafuta  onyeketsera miyambo yonunkha ya makolo awo 

Makhwala a zitsamba: Mlamu wa mfumu anasiya kuona chifukwa choyambana ndi  mfumu. Atachira anaonanso zodabwitsa kamba koti sanamvere malangizo oti asakagone  ndi mkazi wake usikuwo. Panopa akufunafuna sing’anga kuti awapatse mankhwala a  zitsamba. 

  1. Umphawi 

Bambo Gama adapereka Zikani kwa Mgezenge ndi cholinga choti azithandizidwa bwino Makolo a Chisomo anakongola ndalama kwa mkulu wina wolemera. Chifukwa chosowa  ndalama yokabweza, anakapereka Chisomo kwa mkuluyo ngati malipiro 

Zikani asoweka kokatenga ndalama yopereka ku sukulu ya chitukuko ndinso yogula buku  lomwe wophunzira wina anamubera. 

Mayamiko analibe kotenga sopo yochapira zovala zake zakusukulu. Zotsatira zake  akujomba kusukulu. Akudikirira kuti akagula sopo a Mgezenge akumulipira ndalama  pamene wawabweretsera nkhuni. Komabe sanamutse kena kalikonse 

A Mgezenge asawuka kwambiri. Chumna chawo chonse chiwathera. Mapeto ake  akuyendayenda mpaka afika ku nyumba ka Funsani ndi Zikani

error: Content is protected !!
Scroll to Top