Course Content
Kufunika kwa Zisudzo
Chisudzo ndi nkhani yochitika kapena yopeka yomwe imafotokoza zinthu mokhala ngati zikuchitika kumene.
0/2
MITU YONSE MNKHANIYI
0/1
Khoswe Wa Padenga
Kukamba za Bonzo, Goli, Khoswe, Anne ndi Jubeki
0/2
Mudzi Wa Mfumu Tandwe
Kuonongeka kwa zachilengedwe ndi mavuto ena
0/3
CHAMDOTHE NDI ZISUDZO ZINA

NUNSU YOYAMBA  

Bonzo ndi Jubeki athawa kundende 

Chomwe zidachititsa kuti Bonzo ndi Jubeki amangidwe  

Adathyola banki ndipo adaba ndalama zambiri zokwana 200 million kwacha. Zomwe zikadachititsa kuti Bonzo ndi Jubeki agwidwe  

Ganizo la Bonzo loti pothawa kundende avale nsapato: mdidi wawo ukadamveka  Mkuwo wa Bonzo ataponda msomali: atajowa mpanda, Bonzo adakafikira kuponda msomali  ndipo adalira ngati mwana wamng’ono  

Kusiyana kwa Bonzo ndi Jubeki ndi Nyapala pamilandu yawo  

Bonzo ndi Jubeki adathyola banki naba ndalama zambiri; choncho adali akaidi abwinoko.  Nyapala adagwirira kamwana kakang’ono choncho anali mkaidi wachabechabe.  

Maganizo a Bonzo ndi Jubeki pa chitetezo cha ndalama zomwe adabisa  Bonzo anali ndi chikaiko ngati ndalama zomwe adaba nkubisa kumanda zidalipobe popeza  panali patapita zaka ziwiri chikwirireni ndalamazo choncho china chake chikadatha  kuchitika.  

Jubeki adatsindika kuti palibe yemwe akadawadziwa malowo popeza anthu adasiya  kugwiritsa ntchito mandawo.  

Bonzo adatsimikiza nawo mfundoyi ponena kuti palibe yemwe akadadziwa malo omwe anali  pamtunda wa masitepe 77 kuchokera pamtumbira wotsiriza komanso palibe yemwe  akadakumba kumanda.  

Jubeki adakayikira zinthu zotsatirazi: 

Munthu akadatha kuswa mphanje kapena kutsekula munda pamalopo.  Munthu akadatha kumangapo nyumba.  

Ngakhale Jubeki anali ndi nkhawa zimenezi, adalinso ndi chikhulupiriro kuti zimenezi  sizingachitike kumanda  

Umboni woti Bonzo ndi Jubeki adali oopsa komanso adachita umbanda ndi umbava kwa  nthawi yayitali  

Paulendo wothawa kundende, ngakhale munali mumdima, Jubeki adakwanitsa kudziwa  chinthu choopsa chomwe chinali patsogolo pawo chomwe chikadatha kuwavulaza monga  dzenje.  

Jubeki adathawapo apolisi chipolopolo chili pantchafu apolisiwo atamuwombera.  Jubeki adagwira ntchitoyi (umbava ndi umbanda) kwa zaka zoposa makumi awiri.  Bonzo adagwira ntchitoyi kwa zaka khumi ndi mphambu zisanu ndi ziwiri.  

Zomwe Bonzo ndi Jubeki adayenera kuchita kuti asazindikiridwe komanso asagwidwe  Adayenera kupeza zovala zina mwachangu popeza Malaya akundende omwe anali  atavala panthawiyi akadagwidwa nawo poti ngakhale munthu wongodziyendera akadatha  kuwadabwa nkuwagwira.  

Kumbutso  

Bonzo ndi Jubeki adagwirizana zokathyola nyumba yomwe adayiona pafupi n’kulowa  kuchipinda cha makolo kuti akapeze zovala zachimuna.  

Jubeki adauza Bonzo kuti Nyapala adali wopusa zedi popeza adagwirira mwana pamene  azimayi adalipo ambirimbiri omwe akadatha kuwafunsira.  

Kugwirira ana ndi ufiti ndipo anthu amachita zimenezi pofuna zizimba.  

Zipangizo  

  1. Zining’a  

titaya bomwetamweta: titaya mwayi wopezapeza  

tinapakula : tinaba  

walasa : walunjika pa zomwe ndimaganiza  

kamatekenya : munthu wamatekenya  

  1. Zifanifani  

Unafuula ngati mwana wamng’ono: Unafuula mokweza kwambiri kamba ka ululu.  Ukuyenda ngati kamatekenya: Ukuyenda motsimphina kamba ka ululu wakuphazi.  3. Chifaniziro/Chizindikiritso  

Misomali ndi mayenje: Chizindikiritso cha chilango ndinso kugwidwa  4. Msemphano  

Bonzo ndi Jubeki ndi mbala zoopsa zomwe zathawa kundende koma zinali ndi  chikhulupiriro kuti zikapulumuka monga mbala yomwe inapulumutsidwa pamtanda ndi  Yesu nthawi yothaitha. 

  1. Kalosera  

Jubeki adakayikira kuti munthu akadatha kuswa mphanje kapena kutsekula munda  pamalo pamene adafotsera ndalama kapena munthu akadatha kumangapo nyumba. Izi  zidachitikadi. Pamene anthu awiriwa adathawa kundende adakapeza pamalo pamene  adakwirira ndalama patamangidwa chinyumba chachitali.  

Maphunziro m’nunsuyi  

  1. Anthu akuba saopa  

Bonzo ndi Jubeki atathawa kundende adaganiza zothyola nyumba ina kuti apeze zovala  zina kuti asinthe.  

  1. Kulimba mtima  

Bonzo ndi Jubeki adathawa kundende.  

Jubeki adathawa apolisi chipolopolo chili pantchafu atamuwombera.  

  1. Kuganiza mwakuya  

Bonzo ndi Jubeki adaganiza zokabisa ndalama kumanda.  

Bonzo ndi Jubeki adaganiza zoti apeze zovala zina mwachangu poopa kugwidwa ndipo  adagwirizana zothyola nyumba ina nkulowa kuchipinda chamakolo kuti akapeze zovala  zachimuna popeza kuchipinda kwa ana sakadapeza zomwe amafuna.  

NUNSU YACHIWIRI  

Ubwenzi wa Khoswe ndi Anne  

Aliyense mwa awiriwa anali pabanja.  

Anthu awiriwa amapeza danga locheza pamene mamuna wa Anne, Goli, anali mgulu la  anthu okagwira ntchito usiku komanso naye Khoswe amakagwira ntchito yake usiku  (kuyang’anira akayidi).  

Macheza awo amachitikira kunyumba kwa Goli usiku.  

Khoswe amakhotera kunyumba kwa Anne akamapita kuntchito.  

Awiriwa ankalimba mtima nkumacheza mpaka usiku zedi popeza Goli amati akapita  kuntchito ankabwerako 7koloko m’mawa ndipo kunali kovuta kuti wapolisi athawire  kuntchito.  

Tsiku lina Anne adamuphikira Khoswe zakudya zomwe Khosweyo adaziyamikira mpaka  kunyoza mkazi wake ponena kuti Anne pazophika adatha mayunivesite pamene mkazi wake  anali adakali ku pulayimale.  

Chipwirikiti kunyumba kwa Goli  

Akuba adabwera nasolola zovala zomwe zinali pafupi ndi zenera lakuchipinda komwe  Khoswe anali kucheza ndi Anne. Akubawa adasololanso yunifolomu ya Khoswe ya pulizoni.  Khoswe adatchayiridwa thenifolo ndi mzake wakuntchito yomudziwitsa kuti akayidi awiri,  Bonzo ndi Jubeki, adathawa. 

Anne ndi Khoswe adakanika kufuula kuti apolisi awathandize atazindikira kuti  m’chipindamo munabwera akuba poopa kuti akadawululika. Anthu awiriwa ankaopa kuyatsa  getsi m’chipinda momwe ankacheza poopa kuti anthu anyumba yoyandikana ndi ya Goli  komanso alonda a Goli akadakanena kwa Goli.  

Anne adakayikira akayidi omwe adathawa kundende kuti ndi amene adaba zovala kudzera  pazenera pamene iye ndi Khoswe adatanganidwa ndi kucheza.  

Khoswe adavala zovala za Goli zomwe zidali zazikulu zedi ndipo adatuluka n’kumapita.  

Mawu ofunika kuwaona bwino  

  1. Khoswe analidi khoswe.  

Khoswe ankamuzembera Goli nkumachita ubwenzi ndi mkazi wake Anne  chimodzimodzi m’mene amachitira khoswe m’nyumba pozembera mwininyumba  n’kumadya katundu wake.  

  1. Kutchena kapena kukwana kwa zovala ndi pamtendere.  

Khoswe adavala zovala zazikulu zedi zamamuna wake wa Anne popeza adazingwa  pamene akuba adathawitsa yunifolomu yake yakuntchito m’mene iye ankacheza ndi  Anne.  

MFUNDO ZIKULUZIKULU  

  1. Chimasomaso  

Khoswe anali pabanja koma anali kuzemberana ndi Anne mkazi wa Goli.  Anne anali pabanja koma anali kuchita ubwenzi ndi Khoswe yemwe anali pabanja.  2. Mantha  

Khoswe ndi Anne adakanika kuyatsa getsi lam’chipinda momwe ankacheza pamene  amafuna kuti ayang’ane zovala za Khoswe popeza anali kuopa kuti anthu oyandikana  nyumba ndi ya Goli komanso alonda a Goli akadakamuuza bwana wawo.  

Khoswe ankamuopa Goli: ankati ndi wamphamvu zedi mwakuti akangomugwira ndi  Anne mphamvu zonsezo zikadathera pa iyeyo.  

Anne adaganiza zokuwa kuti kudabwera akuba pakutuluka kwa Khoswe m’nyumbamo  popeza ankaopa kuti akadaululika.  

Anne ankamuopa mamuna wake Goli. Pamene Khoswe adamuuza zoti adzayankhe  mamuna wake akabwera pa zakusowa kwa diresi yake yovala pogona komanso zovala za  mamuna wakeyo adati asunga mayankho koma adaonjeza kuti Goli monga wapolisi  amafunsa mafunso akafukufuku kwambiri.  

Matanthauzo amawu  

Uchidzete : uchitsiru  

Duwa, nyale, dzuwa, ngale : mkazi wokongola  

NUNSU YACHITATU 

Kugawana zovala zakuba  

Bonzo ndi Jubeki adazindikira kuti zovala zomwe adaba zinali yunifolomu ya wogwira  ntchito ku pulizoni komanso diresi yovala pogona.  

Jubeki adauza Bonzo kuti iyeyo (Jubeki) ndi yemwe atavale yunifolomuyo popeza adaswa  zenera adali iye ndipo kuti Bonzo avala diresi.  

Anthu awiriwa adagwirizana kuti yunifolomu yaukaidi ayitaye pobisika poopa kuti  kukadakhala kosavuta kuti awalondole.  

Milandu ya bonzo ndi jubeki ndi zilango zake  

Kuthyola banki, kuba ndalama m’banki komanso kuzimbayitsa ndalama.  Bonzo ndi Jubeki adaba ndalama zokwana K200,000,000.  

Mlandu uliwonse unali ndi zaka zake zoti nthu awiriwa akakhale kundende komanso aliyense  mwa iwo adagamulidwa kuti akakhale kundende kwa zaka khumi.  

MFUNDO ZIKULUZIKULU 

  1. Kuganiza mwakuya  

Jubeki adauza Bonzo kuti yunifolomu yaukaidi ayitaye pobisika popeza kuyitaya  pooneka kukadachititsa kuti alondoledwe mosavuta.  

Zipangizo  

Mkuluwiko  

M’mphechepeche mwa njovu sapitamo kawiri: Bonzo ndi Jubeki sanayenera kuthyolanso  nyumba kuti apeze zovala zina popeza akadatha kugwidwa.  

Chining’a  

Makhumutcha Anthu olemera/andalama  

NUNSU YACHINAYI  

Mkazi wa khoswe adabwa ndi mamuna wake  

Anzake a Khoswe adabwera kunyumba namuuza kuti mamuna wake sanali kuntchito. Iye  adadabwa nazo popeza Mwamuna wakeyo adapita kuntchito komweko atavala yunifolomu.  Mwamuna wakeyo adatulukira kunyumba nthawi yomwe anayenera kukhala kuntchito.  Khoswe adatulukira kunyumba atavala zovala zachilendo: chimalaya chachikulu komanso  chibuluku chachikulu.  

Khoswe adamuuza mkaziyo kuti yunifolomu adamutsomphola akaidi omwe adathawa  panthawiyi iye ali kuchimbudzi chapanja.  

Khoswe adaoneka odabwa pamene anzake adamuyimbira foni yomudziwitsa kuti akaidi  athawa. Abwana a Khoswe ndiwo adamudziwitsa mkaziyu.  

MFUNDO ZIKULUZIKULU  

  1. Bodza 

Khoswe adanamiza mkazi wake kuti iye anali kuntchito, adatsekula m’mimba, anali  kuchimbudzi chakunja pamane akaidi ankathawa ndipo akaidiwo adamutsomphola  yunifolomu ali kuchimbudziko, chonsecho Khoswe anali kuchibwenzi (kwa Anne)  komwe yunifolomu yake idabedwa ndi akaidiwo.  

  1. Kuopseza  

Khoswe adaopseza mkazi wake kuti amumenya ngati sasiya kumufunsa.  

Zipangizo: Zining’a  

Mawu oluma: mawu aukali  

Mvumbi wazibakera: zibakera zobwera motsatizana  

NUNSU YACHISANU  

Zokambirana za Goli ndi mkazi wake  

Bodza la Anne kwa mamuna wake Goli  

Adamuuza kuti akuba adaphwanya zenera mpaka kuba iye ali mtulo ndipo akumulota iyeyo  (Goli). Adaonjezanso kuti apolisi amapereka chitetezo kudziko kusiya okondedwa awo  kunyumba.  

Adagwetsa mphwayi mamuna wake pomuuza kuti zojambula zidindo za zala za omwe adaba  m’nyumbamo angozisiya popeza zipangizo zojambulira zinali zodula.  

Mayankho a Goli kwa Anne mkazi wake  

Goli adamuyankha mkazi wakeyo, Anne, kuti kunyumbako adabwerera ntchito komanso  kupereka chitetezo ndi ntchito yomwe adafunsira.  

Adatsimikiza zoti atenga zidindo za zala zakumanja za akubawo ndipo monga wapolisi  ayesetsa kuti akubawo agwidwe. Adafotokozanso kuti ngati si akaidi omwe adathawa ku  pulizoni omwe adaba kunyumbako, adayenera kupeza munthu aliyense yemwe zidindo za  zala zake zikadapezeka kuchipindako.  

NUNSU YACHISANU NDI CHIMODZI  

Bonzo ndi Jubeki agwidwa  

Adafika pamanda pamene adakwirira ndalama zomwe adaba kubanki koma adadabwa ataona  kuti padamangidwa chinyumba chachitali ndipo sakadakwanitsa kuchigwetsa kuti afukule  ndalamazo.  

Mlonda wapamalopo adatchayira lamya apolisi ndipo mkulu wawo (Insipekitala Goli)  adatulukira mwamsanga nawauza anthu awiriwa (Bonzo ndi Jubeki) kuti akuwamanga pa  mlandu wopezeka malo olakwika usiku.  

Chikhothi cholembedwa “Police” chidathandizira Goli kuti azindikire zoti anthu awiriwa  (Bonzo ndi Jubeki) ndi akaidi amene adathawa kundende usiku wapitawo komanso adaba  kunyumba kwake.  

Insipekitala Goli adazindikira kuti anthu awiriwa ndi Bonzo ndi Jubeki pamene Bonzo  adamunong’oneza namuuza kuti akadatha kumulemeretsa usiku womwewo ndi ndalama  zomwe zidali pa chinyumba chachitalipo.  

Kumbutso:  

Jubeki adagonana ndi bwenzi lake (mkazi wapamalo wogulitsa mowa) mosadziteteza  mwakuti anali kukayikira kuti akadatha kumupatsa matenda amakono. Chomwe Jubeki  ankadandaula panthawiyi si matenda amakonowo ayi koma kuwululidwa ndi mkaziyo.  

Jubeki adauza Bonzo kuti akafukula ndalama zomwe adabisa akazisungitsa kwa mkazi  wapamalo ogulitsa mowayo.  

Jubeki adamulonjeza mkaziyo kuti amupatsa ndalama zoti atsegulire malo akeake ogulitsira  mowa.  

MFUNDO ZIKULUZIKULU  

  1. Kusasamala  

Jubeki adagonana ndi bwenzi lake (mkazi wapamalo ogulitsirapo mowa) mosadziteteza.  b. Zinthu zazing’ono zimawululitsa zazikulu  

Chikhothi cholemba mawu oti “Police” chidawululitsa Jubeki ndi Bonzo kuti ndi omwe  adakaba kunyumba kwa Insipekitala Goli.  

  1. Chinyengo  

Bonzo ndi Jubeki adanyengerera Insipekitala Goli kuti ampatsa 50 miliyoni Kwacha  ngati angawasiye osawamanga.  

  1. Kukonda ntchito  

Insipekitala Goli adakana kuchita zachinyengo.  

Ngakhale mkazi wake wa Goli adamugwetsa mphwayi kuti zojambula zidindo za zala za  omwe adaba kunyumba kwawo angozisiya iye adamutsimikizira mkaziyo kuti iye  adabwerera ntchito kunyumbako ndipo ayesetsa kuti okubawa agwidwe.  

Zipangizo  

  1. Chining’a  

Akuthirani machaka: Akuwomberani ndi mfuni  

  1. Msemphano  

Anne adauza Goli mamuna wake kuti akuba adaswa zenera iye ali mtulo akumulota mamuna  wakeyo chonsecho kuba kudachitika iye atatanganidwa ndi kucheza ndi bwenzi lake Khoswe  m’chipinda chomwecho.  

NUNSU YACHISANU NDI CHIWIRI  

Khoswe apanikizidwa ndi Goli kupolisi  

Umboni woti kuthawa kwa akaidi kumamukhudza Khoswe 

Adamizira kuti adadwala mwadzidzidzi panthawi yomwe akaidiwo adathawa koma  atafunsidwa ngati adawadziwitsa abwana ake monga mwa dongosolo la pantchito, iye  adakana. 

Yunifolomu yake yakuntchito idapezeka kunyumba kwa mzimayi woyendayenda yemwe  adapereka zovala kwa Bonzo ndi Jubeki atathawa kundende ndipo chiphaso chake chinali  m’thumba lamalaya.  

Diresi yovala pogona ya mkazi wa Goli yomwe idabedwa kunyumba kwa Goli idapezeka  pamodzi ndi yunifolomu yake ya Khoswe.  

Zovala zomwe zidabedwa kunyumba kwa Goli pamodzi ndi diresi yovala pogona ya mkazi  wake Anne, idapezeka kunyumba ya Khoswe.  

Milandu yomwe Khoswe komanso mkazi wake ankaganiziridwa  

Khoswe:  

Kuthandiza akaidi kuthawa kundende  

Kuthyola nyumba komanso kuba  

Mkazi wa Khoswe:  

Kuthandizira kuba (kubisa zovala zobedwa m’nyumba)  

Kulephera kukanena kupolisi zakatundu wobedwa yemwe adali m’nyumba mwake.  

MFUNDO ZIKULUZIKULU  

  1. a) Bodza  

Khoswe adanama kuti adadwala mwadzidzidzi pamene akaidi awiri ankathawa,  chonsecho anali akucheza kuchibwenzi kunyumba ya Goli.  

  1. b) Chipwirikiti  

Yunifolomu ya Khoswe idapezeka kunyumba kwa mtsikana wapamalo wogulitsa mowa  komanso chiphaso chake chidali m’thumba lamalaya.  

Yunifolomu ya Khoswe idapezeka ndi akaidi othawa kundende.  

Diresi la Anne lovala pogona lomwe lidabedwa kunyumba kwa Goli lidapezeka  kunyumba kwa mtsikana wapamalo ogulitsa mowa.  

Zovala za Goli zomwe zidabedwa kunyumba kwake, zidapezeka kunyumba kwa  Khoswe.  

Zipangizo  

  1. a) Msemphano  

Goli adauza Khoswe kuti chitsimikizo choti iye (Khoswe) adali ndi akaidi ndi choti  atavula yunifolomu yake n’kuwapatsa akaidiwo, iwo adamupatsa malaya ake (a Goli) omwe adaba kunyumba kwake kuti iye asayende maliseche. Zoona zake n’zakuti akaidi  adaba yunifolomu ya Khoswe pamene iye adatanganidwa ndi kucheza ndi Anne  m’chipinda chomwe mudabedwamo ndipo Anne ndi yemwe adampatsa Khoswe zovala  za Goli kuti avale. 

Mkazi wa Khoswe adaganiziridwa mlandu wobisa katundu wobedwa komanso kulephera  kukanena kupolisi zakatundu wobedwa yemwe adali m’nyumba mwake. Zoona zake  n’zakuti zovala za Goli zomwe zidapezeka m’nyumba mwake sizidabedwe; mamuna  

wake Khoswe adabwera atavala zovala za Golizo usiku tsono kunali kovuta kuti mkazi  wa Khoswe akanene kupolisi. 

  1. b) Chining’a  

Ndikuchotsa chimbenene: Ndikukhaulitsa zedi.  

NUNSU YACHISANU NDI CHITATU  

Kubwalo lamilandu: chilungamo chidziwika  

Mkazi wa Goli, Anne, adauza woweruza kuti adali ali mtulo pomwe akuba adaswa zenera  ndipo adazindikira kutacha kuti magalasi anali ataphwanyidwa komanso zovala za mamuna  wake zidabedwa pamodzi ndi diresi lake lovala pogona.  

Bonzo adavomereza mlandu wothawa kundende osati wolanda Khoswe yunifolomu. Iye  adafotokoza kuti atathawa kundende adaphwanya zenera pa nyumba ina momwe adabamo  zovala ndipo adazindikira kuti panali yunifolomu ya msirikali wandende ndi diresi lovala  pogona. Pamene ankaba zinthuzi n’kuti bambo ndi mayi a m’nyumbamo akucheza  mwachikondi pa kama. Yunifolomu yomwe adatengayo adakasungitsa kwa bwenzi lake ku  bala.  

Jubeki nayenso adavomera mlandu wothawa kundende osati wolanda Khoswe yunifolomu.  Iye adafotokoza kuti ntchito yake inali yoonetsetsa ngati sikumabwera anthu panthawi  yomwe Bonzo amaswa zenera. Nayenso adanena kuti eni nyumbayo anali akucheza pa kama  m’mene iwo ankaba. Iye adati adamuzindikira mkazi wa Goli koma mamuna yemwe  annkacheza naye sadamuzindikire.  

Khoswe adauza woweruza kuti akudziwa Bonzo ndi Jubeki osati mkazi wa Goli. Jubeki ndi  Bonzo adathawa kundende ndipo adamulanda yunifolomu iye akudzithandiza atadwala  m’mimba mwadzidzidzi. Iye adadzikola ponena kuti sadamuone Bonzo pamene amaswa  zenera kunyumba ya Goli komanso adakanika kumuyankha Bonzoyo pamene adamufunsa  ngati adayamba wajambulitsapo ndi mkazi wa Goli. Khoswe adanenetsa kuti Mayi Goli  sanali kuwadziwa.  

Jubeki adawulula kuti sadamutsomphole Khoswe yunifolomu. Iye ndi Bonzo adaba  yunifolomu kunyumba ya Goli ndipo m’thumba la yunifolomuyo dapeza chithunzi.  Adapereka chithunzicho kwa woweruza milandu. (Khoswe ndi Anne adakumbaturana  mwachikondi pachithunzipo.)  

Kumbutso: Goli sankadziwa kuti kunyumba kwake kudalowa mamuna wina yemwe  ankazemberana ndi mkazi wake Anne koma zoyankhula za Bonzo ndi Jubeki zidawulula za  mamunayu.  

Zipangizo  

  1. a) Chining’a: Mumakadzithandiza  
  2. b) M’malere/M’biso: Mlembi sadafotokoze zomwe Goli adachitira mkazi pamene adazindikira  kuti anali ndi mamuna wina iye ali kuntchito.  

Makhalidwe oipa mu seweroli ndi zotsatira zake

Khoswe athawa kuchokera ku ntchito yoyang’anira akaidi napita ku chibwenzi chake, Anne,  mkazi wa Inspector Goli, zotsatira zake Bonzo ndi Jubeki apezerapo mpata nathawa ku  ndende kuja 

Khoswe ali kwa Anne, Bonzo ndi Jubeki amubera shati ndi buluku lake (uniforomu ya  pulizoni), mapeto ake ayenda atamvala Malaya a Inspetor Goli. 

Bonzo ndi Jubeki athyola banki nabamo ndalama zokwana k200 miliyoni ndipo azibisa ku ku  manda, masitepe 77 kapena malipande makumi asanu kuchokera pa mtumbira womaliza.  Pothawa kuchokera ku ndende apeza anthu atamangapo kale nyumba, komanso apolisi  awagwiranso. 

Bonzo ndi Jubeki athawa kuchokera ku ndende ndipo apita kumanda kuja kuti akafukule  ndalama zawo. Koma mlonda wa ku nyumba yomwe inamangidwa pomwe anabisa ndalama  zawo ayimbira foni apolisi omwe abwera nawakwizinganso kachikena  

Akuthawa ku ndende Bonzo ndi Jubeki, Bonzo anaponda msomali nafuula ndi ululu, mapeto  ake amayenda motsimphina. Komanso, akuyenda ayandikira nyumba ina naganiza kuti  abemo zovala, Jubeki nayenso aponda msomali koma azulidwa ndi mnzake. 

Pothawa, Jubeki anati mkaidi wina (nyapala) anali mu ndende chifukwa chogwirira ka  mwana kakang’ono. 

Padziko la pansi palibe chinsinsi (Chilichonse chimaululika) 

Khoswe anathawa ku ntchito napita kwa Anne. Bonzo ndi Jubeki atathawa, Goli apita  kunyumba kwa mkazi wa Khoswe kukamufunafuna. Khoswe nayenso afika atavala malaya  ena. Izi zidabwitsa mkazi wake pa za komwe anali.  

Bonzo ndi Jubeki aba ndalama ku banki nazibisa ku manda, malipande 50 kuchokera pa  mtumbira womaliza. Palibe amene anauziwa za idzi. Koma pokazitenga agwidwa ndipo  amuuza Goli za izi. 

Pothawa ku ndende, Bonzo ndi Jubeki asungitsa zovala zomwe adakaba kwa Goli kwa  msungwana wina wogwira ntchito ku malo ogulitsira mowa. Koma mzimayiyo amugwira  apolisi ali ndi uniforomu ya pulizoni 

Zovala za goli zipezeka kunyumba kwa khoswe. Ndipo uniforomu ya Khoswe ipezeka ku  nyumba kwa msungwana woyendayendayu yemwe amagwira ntchito ku malo ogululitsira  mowa 

Pa tsiku la mlandu, Bonzo ndi Jubeki akana kuti sanawatsomphole zovala Bambo Khoswe  koma awuza khoti kuti anaziba ku nyumba ina komwe banja (khoswe ndi Anne) limacheza  pa bedi.  

Jubeki awonetsa khoti chithunzi chomwe pali mayi Goli ndi bambo Khoswe. Jubeki awuza  khotilo kuti chithunzicho chinapezeka mu thumba la thalauza la Khoswe

error: Content is protected !!
Scroll to Top