Course Content
Kufunika kwa Zisudzo
Chisudzo ndi nkhani yochitika kapena yopeka yomwe imafotokoza zinthu mokhala ngati zikuchitika kumene.
0/2
MITU YONSE MNKHANIYI
0/1
Khoswe Wa Padenga
Kukamba za Bonzo, Goli, Khoswe, Anne ndi Jubeki
0/2
Mudzi Wa Mfumu Tandwe
Kuonongeka kwa zachilengedwe ndi mavuto ena
0/3
CHAMDOTHE NDI ZISUDZO ZINA

NUNSU YOYAMBA  

Kunyumba kwa Ndileya  

Ndileya akufika kumene kunyumba kuchokera kodula nsungwi adapeza mkazi wake  Nadzonzi kulibe ali kuchitsime kotunga madzi. M’kudziyanhulira kwake, Ndileya adaulula  kuti pakhomo sipanali bwino:  

Nkhuku zinali balala.  

Mbuzi zinali kunja pachingwe.  

M’yumba munali mosasesa.  

Mabulangeti anali okuda kwambiri.  

Makhalidwe a Nadzonzi  

Kumwa mowa  

Kuchita miseche  

Ulesi  

Kusasamala zinthu ndi ana  

Umboni woti Nadzonzi anali mlesi komanso mtchisi  

Adakhala zaka zitatu osachapa mabulangeti.  

Mamuna wake adampatsa sopo koma samachapa zovala.  

Chilundu chomwe adavala panthawiyi chinali nakanaka.  

Adakhala kwa mwezi wathunthu osasesa m’nyumba.  

Sadaphikire ana mpaka adachoka pakhomo.  

Umboni woti Ndileya ankamumenya Nadzonzi  

Pamene Nadzonzi adamuuza Ndileya kuti adachedwa kuchitsime popeza chidayamba  kuphwa mwakuti ankachita kudikira kuti madzi adzadze, Ndileya sadakhutire ndipo  adamuuza Nadzonzi kuti ichi ndi chifukwa chomwe adapeza.  

Nadzonzi adapepesa nati m’mene anamumenyera sabata yapitayo sanali kupeza bwino  mwakuti sakadatha kuyenda mwachangu.  

Kumbutso:  

Ndileya adauza Nadzonzi kuti utchisi wake wamukwana ndipo m’kuyankhula kwake  adasonyeza kuti ankalakalaka atapeza mkazi wina.  

Zomwe zidasonyeza kuti Ndileya ankafunadi mkazi wina  

Adamuyerekeza mkazi wake ndi duwa lofota ndi dzuwa ndipo adamuuza kuti ankafuna  kaduwa katsopano kosiyana ndi Nadzonziyo.  

Adati mkazi watsopano akadatha kusamala m’nyumba ndi zinthu mwaukhondo.  Adatsindika kuti adatopa ndi moyo wankhumba (wauve). 

Adanenanso kuti m’nyumba mwake mumafanana ndi m’khola poti munali mwanyansi:  zinthu zinali mbwee.  

Chipanda chamowa chidzetsa mkangano pakati pa Nadzonzi ndi mamuna wake Ndileya  Ndileya adakayikira kuti Nadzonzi adamuyikiramo mankhwala m’chipandamo popeza  chidagwa n’kusweka iye atangoyamba kumwa komanso mumaoneka tinthu takuda.  Ndileya adafunsa Nadzonzi ngati sadamuyikire chiphe m’mowawo koma Nadzonzi  adakanitsitsa.  

Nadzonzi adauza mamuna wakeyo kuti mowawo adapatsidwa ndi Nasiwelo. Ndileya  adakwiya kwambiri ndi nkhaniyi popeza Nasiwelo ankatchuka ndi mchitidwe wopeperetsa  amuna okwatira.  

Ndileya adamuopseza mkazi wake Nadzonzi ndi mpeni mpaka adaulula kuti adamuyikira  mankhwala m’mowawo. Iye adati adachita zimenezi kuti Ndileya abwerere kwa iye kuchoka Nanzunga.  

Kumbutso:  

Ndileya adayitanitsa Nachuma (mchemwali wake wamkulu wa Nadzonzi) kuti adzamve  zomwe adachita mchemwali wake.  

Nachuma ataona kuti sayikwanitsa yekha nkhaniyo, adapempha Ndileya kuti apite  akawafotokozere atsibweni ake a Nadzonzi a Chidazi.  

Nadzonzi adayankhula kuti Ndileya anali ndi chikondi chabodza: analonjeza zomukonda  Nadzonzi pachisoni ndi pachimwemwe koma panthawiyi anali kuzemberana ndi  Nanzunga mwakuti sanali kumulabadiranso iye monga mkazi wake.  

Zipangizo  

  1. Voko : Mtolo wansungwi uli panjapo wandiphadi.  
  2. Zining’a  

Pali kangaude pam’mero panga: Ndili ndi chipemba kwambiri 

Inetu sindipindira iwe manja anga: Inetu sindigwirira iwe ntchito.  

Moyo wankhumbawu: Moyo wauvewu/ moyo wautchisiwu  

Moti mutha kundigeya?: Moti mutha kundisiya banja?  

MFUNDO ZIKULUZIKULU  

  1. Utchisi 

Nadzonzi adakhala zaka zitatu osachapa mabulangeti.  

Ndiliya adampatsa sopo Nadzonzi koma samachapa zovala.  

Chilundu chomwe adavala Nadzonzi panthawiyi chinali nakanaka.  

Nadzonzi adakhala kwa mwezi wathunthu osasesa m’nyumba.  

  1. Zikhulupiriro  

Ndileya adakhulupirira kuti mkazi wapabanja akamacheza ndi mbeta ndiye kuti  akukhalira miseche. 

Ndileya adakhulupirira kuti Nadzonzi anamuyikira mankhwala (mkala wamchira  wabuluzi) m’mowa pamene chipanda chidagwa n’kusweka iye atangoyamba kumene  kumwa mowa.  

  1. Kunyoza  

Ndileya ankamutcha Nadzonzi mlesi, chidzete komanso mtchisi.  

  1. Nkhanza  

Ndileya adamenya mkazi ndipo mkaziyo adavutikabe kwa masiku angapo kuti akwanitse  kuyenda mwachangu.  

NUNSU YACHIWIRI  

Kunyumba kwa a Chidazi  

Ndileya adafikako mwaukali akumunyoza Nadzonzi kuti ndi chidzete komanso  adadumpha malire. Iye adauza a Chidazi kuti mdzukulu wawo adamuthirira mkala  wamchira wabuluzi m’mowa.  

Zotumphuka m’nunsuyi  

A Chidazi ankadziwa kuti Ndileya amamumenya mkazi wake.  

Ndileya sanali kuwawopa a Chidazi.  

Matanthauzo a mawu  

Chidzete : chitsiru  

Wadumpha malire : waonjeza  

NUNSU YACHITATU  

Kunyumba kwa Ndileya  

A Chidazi adziwa chilungamo  

Adafunsa mdzukulu wawo Nadzonzi kuti afotokoze chomwe chidamuchititsa kuti athirire  mamuna wake mkala wamchira wabuluzi m’mowa.  

Poyamba Nadzonzi adanama kuti ndi Nasiwelo yemwe adamunyenga zoti athirire Ndileya  mankhwala m’mowa.  

Nadzonzi adauza atsibweni akewo kuti adamuthirira Ndileya mkala wamchira wabuluzi m’mowa popeza amafuna kuti abwerere kwa iye; achoke kwa Nanzunga komwe ankagona  usiku uliwonse.  

Nadzonzi adafotokozera atsibweni akewo kuti mwezi udatha mwamuna wake asakugona  m’nyumba mwake koma ankakagona kwa Nanzunga ndipo Nasiwelo adamulangiza kuti atha  kukhwimitsa chikondi chake ndi Ndileya mamuna wake pomupatsa mankhwala achikondi. 

Pamfundozi a Chidazi adayankha zotsatirazi:  

Nasiwelo adamunamiza Nadzonzi (adamunyenga kudya nyama yagalu) mwakuti adakwiyitsa  mamuna wake (adaponya muvi mumtima mwa mwamuna wake.)  

Nadzonzi akadawadziwitsa ndipo akadapeza njira yabwino yothetsera vutoli. 

Pamene Ndileya adamva mawu a Nadzonzi (kuti iye adamupempha mankhwala Nasiwelo)  adamuthamangitsa ndipo adamunyoza kuti ndi mdyerekezi komanso ndi wodetsedwa. Iye  adati sadagwiritse ntchito mankhwala kuti Nadzonzi amulole.  

Zotumphuka m’gawoli  

Akazi ndi ogona popeza amatsatira zilizonse zomwe amawanong’oneza anthu amene amati  ndi anzawo; makamaka amene amasangalatsidwa ndi mjedo. (mawu a a Chidazi komanso  Ndileya)  

NUNSU YACHINAYI  

Ku bwalo lamilandu  

Mfumu idathokoza anthu kamba kobwera kumilandu m’malo mopita kukakolola.  Madandu a Ndileya pabwalo lamilandu  

Akuzunzika kwambiri ndi Nadzonzi.  

Nadzonzi sasesa m’nyumba (wakhala mwezi wathunthu osasesa m’nyumba)  Nadzonzi sadalotche zipupa kuchokera tsiku lomwe adakwatirana.  

Nadzonzi sachapa zovala ngakhale amamugulira sopo.  

Nadzonzi saphikira ana.  

Nadzonzi amachoka pakhomo m’mawa nkumakabwera madzulo.  

Nadzonzi sasiya madzi panyumba/pakhomo.  

Nadzonzi adamuthirira mkala wamchira wabuluzi m’mowa.  

Mawu a Nachuma, mboni ya Ndileya  

Adauza bwalo kuti padalibe aliyense pamene Nadzonzi ankapereka mowa kwa mamuna  wake.  

Adavomereza kuti Nadzonzi adathirira mamuna wake mankhwala m’mowa.  Iye adauza bwalo kuti ngakhale iye kudalibe, koma Nadzonzi mwini wake adavomereza kuti  adayika mankhwala m’mowa womwe adapereka kwa mamuna wake Ndileya.  Adatsimikizira bwalo kuti mkala womwe unathiridwa m’mowa sunali mwaye popeza unali  ndi mphumphu zazikuluzikulu kuposa mwaye.  

Madandu a Nadzonzi  

Mamuna wake Ndileya amamumenya sabata iliyonse pofuna kumuchititsa kuti amusiye.  Ndileya amafuna kukwatira Nanzunga; adamugulira nyama yang’ombe kambirimbiri pamene  iye ndi ana ake ankadyera mnkhwani.  

Akaphika nsima, Ndileya amangodya mwapatalipatali.  

Ndileya wakhala akugona kwa Nanzunga kwa sabata zambiri.  

Ndileya amamunyoza komanso amamukwiyira kawirikawiri.  

Mawu a Chidazi mboni ya Nadzonzi  

Ndileya ndi wankhanza komanso wautambwali. 

Ndileya amamumenya mkazi wake mwakuti mkaziyo wakhala akudandaula.  Nadzonzi sadamuuze zoti mamuna wake Ndileya akuyenda ndi Nanzunga.  Nadzonzi akutayirira pankhani yogwira ntchito pakhomo monga kusesa m’nyumba popeza  akukhumudwitsidwa ndi khalidwe la Ndileya.  

Umboni woti Nadzonzi ankamenyedwa ndi mamuna wake Ndileya  

Mkono wake wamanja unali wosupuka.  

Anali ndi zipsera pachipumi chake.  

Anali ndi bala pamsana pake.  

Mayankho a Ndileya kwa mfumu pankhani yomenya Nadzonzi komanso kuchita ubwenzi  ndi Nanzunga  

Adavomera nkhanizi ndipo adati:  

Nandzonzi ndi amene amamuchititsa kuti azimumenya.  

Nadzonzi ndi cholengedwa chopusa komanso chamtima wapachala (wosachedwa kukwiya).  

Malangizo amfumu asanapereke chigamulo  

Kwa Nadzonzi  

Aziuza atsibweni ake mamuna wake akamulakwira ndipo ngati sakuyanjana kwa atsibweni  ake azikagwada kubwalo lamilandu.  

Sakuyenera kupereka yekha chigamulo monga adachitira pothirira mamuna wake mankhwala m’mowa.  

Asamagwiritse ntchito mankhwala pofuna kuti mamuna wake amukonde.  Chikondi sagula, sakakamiza komanso sapanga ngati zidole.  

Chikondi ndi mphatso yachilengedwe yochokera kwa Chiuta.  

Kwa Ndileya  

Azidziwitsa atsibweni ake a mkazi wake ngati mkaziyo walakwitsa kanthu.  Adachita zachibwana pozemberana ndi Nanzunga.  

Akhale wokhulupirika kwa mkazi wake ndipo ndi wake mpaka muyaya.  

Chigamulo chamfumu  

Sadapeze zifukwa zokwanira zothetsera banja la Ndileya ndi Ndzonzi.  Ndileya ayanjane ndi mkazi wake Nadzonzi.  

Nandzonzi apereke dipo la mbuzi kubwao la mfumu kamba kophwanya malamulo amudzi  pomuthirira mankhwala mamuna wake m’mowa.  

Ndileya salandira kanthu kuchokera kwa mkazi wake m’malo mwake abwerere kunyumba  azikakhala naye.  

Ndileya azikumbukira kuti kumenya sikumasandutsa chinthu choyipa kukhala chabwino.  Zipangizo 

26 

  1. Mkuluwiko  

Wamva m’mimba ndiye atsekula chitseko: Amene ali ndi vuto ndi yemwe amasaka  thandizo.  

  1. Zining’a  

Bwalo ndilo liphwanye mutu wanyani: Bwalo ndilo lipereke chigamulo kapena chilango.  Chamtima wapachala: Chosachedwa kukwiya kapena kunyanyala  

Ziphaliwali: Ukali kapena kulalata  

Igwa apa: Lipira  

MFUNDO ZIKULUZIKULU 

  1. Nkhanza 

Ndileya ankamumenya mkazi wake Nadzonzi mwakuti adasupuka pamkono, adali ndi  zipsera pachipumi komanso anali ndi bala kumsana. Kumenyedwaku kudachititsa  Nadzonzi kuti akanike kuyenda mwachangu pochokera kuchitsime kotunga madzi.

2. Kupirira 

Ngakhale Nadzonzi ankachitidwa nkhanza ndi mamuna wake (kumumenya komanso  kuzemberana ndi Nanzunga) iye sadathetse banja ndi mamuna wake Ndileya. Iye adauza  bwalo kuti amamukondabe Ndileya. 

  1. Chilungamo 

Amfumu adagamula kuti Ndileya ayanjane ndi Nadzonzi mkazi wake ndipo kuti iwo  sadapeze zifukwa zokwanira kuthetsa banja la anthu awiriwa. 

Nadzonzi adavomera kuti adathira mankhwala m’mowa womwe adapereka kwa  mwamuna wake Ndileya pofuna kuti Ndileya asiye kupita kwa Nanzunga. Ndileya adamuuza Nadzonzi kuti adatopa ndi utchisi komanso ulesi wake mwakuti anali  kufuna kukwatira mkazi wina yemwe angathe kusunga m’nyumba ndi katundu  mwaukhondo. 

Nachuma adauza bwalo kuti padalibe munthu wina aliyense pamene Nadzonzi  ankapereka mowa kwa mamuna wake Ndileya. Zoti anathira mkala wamchira wa buluzi  mmowa womwe adapereka kwa mamuna wake adadziwa popeza adawona mkalawo  komanso mwini wakeyo, Nadzonzi adavomera kuti adathiramo mankhwalawo. 

Amalume ake a Nadzonzi, a Chidazi adauza bwalo kuti Ndileya amamumenya mkazi  wake ndipo adaonetsa zipsera zomwe zinali pachipumi pa Nadzonzi, bala lomwe linali  pamkono wake komanso kumsana kwake. 

  1. Banja si mankhwala 

Mankhwala omwe Nadzonzi adakatenga kwa Nasiwelo nathirira Ndileya m’mowa kuti  Ndileyayo achoke kwa Nanzunga n’kubwerera kwa iye sadagwire ntchito m’malo;  mwake Ndileya adakasuma kubwalo lamilandu kwa amfumu kupempha kuti amusiye  Nadzonzi. 

  1. Kulephera udindo

A Chidazi ankadziwa ndipo anali ndi umboni woti Ndileya ankamuchitira nkhanza  mdzukulu wawo Nadzonzi koma palibe chomwe adachitapo monga kukasuma kubwalo  lamilandu. M’malo mwake adakapereka umboniwu pamene Ndileya adakadandaula  kubwalo lamfumu kuti akufuna kumusiya banja Nadzonzi ndipo akufuna kukwatira  mkazi wina. 

A Chidazi adakanika kuganiza mwakuya kuti aweruze nkhani ya mdzukulu wawo  Nadzonzi ndi mamuna wake Ndileya. Iwo adangokhulupirira kuti Nadzonzi adalakwa  koma sadafune kuunika bwinobwino chomwe chidachititsa Nadzonzi kuti amuyikire  Ndileya mankhwala m’mowa. Adayankhula kuti akazi ndi ogona popeza amatsatira  zilizonse zomwe amanong’onezedwa ndi anthu omwe amati ndi anzawo. Bambowa  adakanika kumuuza Ndileya kuti nayenso anali olakwa m’malo mwake adauza Ndileya  kuti iwo amusunga Nadzonzi mpaka tsiku lamilandu. 

Nadzonzi amakanika kuwaphikira ana asanachoke pakhomo. Monga mkazi wapabanja  komanso mayi wa ana, Nadzonzi anayenera kuonetsetsa kuti ana adya asanapite  kosewera komanso anayenera kudziwa komwe ana ake akupita. Ana a Nadzonzi  adachoka osadya popita kukacheza ndipo amayi awo samadziwa komwe adalowera  mpaka dzuwa lidalowa. 

Mawu ena ofunika kuwawunikira 

  1. Umanena chatsitsa dzaye kuti njovu ithyoke mnyanga 

Ulesi ndi utchisi wa Nadzonzi udachititsa kuti Ndileya ayambe kuyenda ndi Nanzunga  ndipo adakhulupirira kuti mkazi watsopanoyu angathe kusamala mnyumba komanso  zinthu mwaukhondo. 

Mayendedwe a Ndileya ndi omwe adachititsa Nadzonzi kuti asakesake mankhwala  n’kumuthirira mamuna wakeyo m’mowa ngati njira imodzi yolimbitsira chikondi chawo. 

2. Mfumu idagamula bwino mlanduwu 

Adafufuza bwinobwino mlandu womwe Ndileya adasumira mkazi wake Nadzonzi ndipo  adapereka chigamulo choyenera.  

Sadathetse banja la Ndileya ndi Nadzonzi monga amafunira Ndileya.  Adapereka malangizo abwino kwa anthu onse awiriwa (Ndileya ndi Nadzonzi) nawauza  kuti ayanjane. 

  1. Zivumbulutso: Zinthu zomwe zidachititsa kuti zinthu zina zobisika zibwere poyera.
  2. a. Kugwa ndi kusweka kwa chipanda chamowa 

Kupulumuka m’manja kwa chipangizochi, Ndileya atangoyamba kumwa mowa,  komanso kusweka kwake kudachititsa kuti Ndileya akayikire zoti Nadzonzi  adamuyikira mankhwala m’mowa. 

Kusweka kwa chipangizochi kudachititsa kuti mkala wamchira wabuluzi womwe  Nadzonzi adathira m’mowa uwoneke ndipo Ndileya adakwiya kwambiri. 

b. Mpeni 

Ndileya atamufunsa Nadzonzi kuti awulule yemwe adathira mankhwala m’mowa, iye  adakanitsitsa kuti sakudziwa. Pamene Ndileya adatenga mpeni n’kumuuza mkazi  wakeyu kuti amupha nawo akapanda kuwulula yemwe anathira mankhwala m’mowa,  iye (Nadzonzi) adawulula kuti adathira ndi iyeyo  

  1. Kupempha chisudzulo  

Pamene Ndileya adayala madandaulo ake kubwalo lamilandu n’kupempha kuti  amusiye Nadzonzi makamaka chifukwa adamuthirira mankhwala m’mowa, Nadzonzi  adaulula kuti adamuthirira mankhwala achikondi popeza ankayenda ndi mkazi wina,  sankagona pakhomo komanso samamusamala pamodzi ndi ana ake omwe.  

Nadzonzi adaululanso kuti Ndileya amamumenya sabata iliyonse. Mboni ya  Nadzonzi idaonetsa mkono wosupuka wa Nadzonzi, zipsera pachipumi pake komanso  bala kumsana kwake.  

Kusumaku kudaululitsanso kuti Ndileya adamugulira Nanzunga nyama yang’ombe  kambirimbiri pamene iye ndi ana ake ankadyera nkhwani.  

  1. Mtsiriko womwe Ndileya adapatsidwa ndi malemu bambo ake  

Mtsiriko umenewu udathandizira kuti Ndileya adabwe ndipo azindikire kuti china  chake chinayikidwa m’mowa womwe adapatsidwa kuti amwe.  

Makhalidwe a Nadzonzi 

  1. Waulesi 

Mu khitchini mumakhala mopanda madzi. Mu nyuma mumakhala mosasesa Mabulangete ndi akuda kwambiri ndipo osachapidwa kwa zaka zitatu 

Amalephera kuchotsa mbuzi pa zingwe 

  1. Wosasamala banja: Akamachoka pa khomo sasiya chakudya kuti mwamuna wake  akabwera azichipeza 
  2. Wogonjera: Mwamuna wake amukalipira chifukwa chofika mochedwa ku chokera ku  madzi. Iye apempha Ndileya kuti amukhululukire. Ati akukanika kuyenda msanga chifukwa  chomenyedwa ndi mwamuna wake 
  3. Wachikondi: Athira mankhwala a mchira wabuluzi mu mowa kuti mwina mwamuna wake  azimukonda kwambiri. Asiye kupita kwa Nanzunga 
  4. Wopusitsidwa: Apusitsidwa ndi nasiwero kuti atenge mchgira wa buluzi kuti athire mu  mowa. Akatero mwamuna wake azimukonda kwambiri 
  5. Wa chilungamo: Avomera pa bwalo la mfumu kuti anathiradi mchira wa buliuzi mu mowa  ndi chiolinga choti Ndileya azimukonda kwambiri, asiye kumumneya komanso amusiye  Nanzunga 

Makhalidwe a Ndileya 

  1. Wa ndeu 

Amenya mkazi wake chifukwa chothira mchira wa buluzi mu mowa 

Amenya ndikusupula mkono wakumanja wa Nadzonzi

Apatsa mkazi wake zipsera pamphumi chifukwa chomumenya 

  1. Wachimasomaso: Nthawi zambiri amachoka usiku kunyumba kwake napita kwa Nanzunga,  chibwenzi chake. Ananena izi ndi Nadzinzi ku bwalo la milandu 
  2. Wopanda ulemu 

Sakuwapatsa ulemu atsibweni ake pamene anapita kuti akawawuze zomwe mkazi wake  anachita pothira mchira wa buluzi mu mowa 

Achita kunjenjemera ndi mantha komanso ukali pamaso pa atsibweni ake nawauza kuti  mudzaone zochita za chidzete chanu 

  1. Wosakhululuka mnsanga: Awuza Nadzonzi pamaso pa atsibweni ake azipita chifukwa  chothira mchira wa buluzi mu mowa 
  2. Wolimbikira: Agwira ntchito molimbika mu minda yachimanga kuti adyeste ana ake. Sopo  amagulanso. Ananena izi pabwalo la mfumu. Koma mkazi wake amalephera kudzigwiritsira  ntchito bwino
error: Content is protected !!
Scroll to Top