Course Content
Kufunika kwa Zisudzo
Chisudzo ndi nkhani yochitika kapena yopeka yomwe imafotokoza zinthu mokhala ngati zikuchitika kumene.
0/2
MITU YONSE MNKHANIYI
0/1
Khoswe Wa Padenga
Kukamba za Bonzo, Goli, Khoswe, Anne ndi Jubeki
0/2
Mudzi Wa Mfumu Tandwe
Kuonongeka kwa zachilengedwe ndi mavuto ena
0/3
CHAMDOTHE NDI ZISUDZO ZINA

MAFUNSO OYANKHA MWACHIMANGIRIZO 

  1. Kodi chisudzo cha Mchira wa buluzi ndi Zikani zikufanana bwanji? Fotokozani mfundo  zinayi
  2. Fotokozani zochitika zomwe zikutsimikizira kuti mlembi adagwiritsa ntchito msemphano  m’zisudzo izi:  

Chamdothe, Khoswe wapadenga ndi Zikani  

Chamdothe 

  1. Tsimikizani polemba mfundo zinayi kuti atengambali ena anali ankhanza 2. Fotokozani mfundo zinayi zotsimikiza kuti ampangankhani ena anali a makhalidwe abwino 

Mchira wa buluzi 

  1. Tsimikizani polemba mfundo zinayi kuti atengambali ena adali odekha pochita zinthu
  2.  Fotokozani mfundo zinayi zotsimikiza kuti ampangankhani ena anali a makhalidwe oipa
  3. Tsimikizani popereka mfundo zinayi zowonetsa kuti mkazi wopusa amapasula banja ndi  manja ake. 
  4. Fotokozani mfundo zinayi zosonyeza kufunika kwa zivumbulutso m’chisudzochi. 
  5.  Fotokozani mfundo zinayi zotsimikiza kuti Ndileya adali wachikondi pa mkazi wake Nadzonzi. 

Khoswe wa padenga

  1. Tsimikizani polemba mfundo zinayi kuti amapangankhani ena anali osakhulupirika
  2. Tsimikizani pofotokoza mfundo zinayi kuti choipa chitsata mwina 
  3. Tsimikizani mawu oti atambwali sametana polemba mfundo zinayi 
  4. Fotokozani mfundo zikuluzikulu zinayi zopezeka mu chisuzochi  

Zikani  

  1. Fotokozani mfundo zinayi zosonyeza kuti aliyense amakolola zomwe wafesa
  2. Tsimikizani pofotokoza mfundo zinayi kuti choipa chitsata mwini. 
  3. Fotokozani mavuto anayi omwe bambo Mgezenge adakumana nawo kamba ka makhalidwe  awo oipa  
  4. Ndi zochitika zinayi ziti zomwe zikusonyeza kuti Mgezenge anali wankhanza? Fotokozani. 

Mudzi wa Mfumu Tandwe 

  1. Tsimikizani polemba mfundo zinayi kuti mu nkhaniyi munali nkhanza
  2. Fotokozani makhalidwe anayi oipa ma mu chisudzochi  
  3. Fotokozani mfundo zikuluzikulu zinayi zopezeka mu chisudzochi 
  4. Ndi zinthu zinayi ziti zomwe zikusonyeza kuti zinthu sizimayenda bwino m’mudzi mwa  Mfumu Tandwe ngakhale munali dongosolo? Fotokozani.
error: Content is protected !!
Scroll to Top