Course Content
Kufunika kwa Zisudzo
Chisudzo ndi nkhani yochitika kapena yopeka yomwe imafotokoza zinthu mokhala ngati zikuchitika kumene.
0/2
MITU YONSE MNKHANIYI
0/1
Khoswe Wa Padenga
Kukamba za Bonzo, Goli, Khoswe, Anne ndi Jubeki
0/2
Mudzi Wa Mfumu Tandwe
Kuonongeka kwa zachilengedwe ndi mavuto ena
0/3
CHAMDOTHE NDI ZISUDZO ZINA

KUBWALO LA MFUMU TANDWE  

Chiphaliwali adaletsa phokoso ndipo adauza anthu kuti msonkhano udayenera  kuyambika.  

Cholinga chamsonkhano  

Kukambirana/kuunikira mfundo zofunika kwambiri m’mudzimo  

Mawu amfumu potsekulira msonkhano  

Adayamikira anthu kuti zomwe adagwirizana pamsonkhano ngati womwewu chaka  chapitacho zinali kuchitika ndipo anthu andayambapo kuona zipatso zake.  M’chaka chatsopanochi, anali ndi mitu ingapo yoti akambirane. 

Idayitana nduna zake kuti zifotokoze mitu yomwe idalipo motere:  

MAYI CHIBWE  

Adayankhula zinthu zokhuza kuonongeka kwa chilengedwe zotsatirazi:  

Mvula yayambanso kugwa mwa njomba 

Mudzi wawo unali wochita bwino (wa mwanaalirenji)  

Anthu ochokera kumadera ena monga ku Chombo, ku Linga, kwa Kalimanjira, ku  Chithiba ndi ku Benga ndi ena ochokera kumapiri ankadzachita nsuma. Anthuwa  ankatsata zakudya monga chimanga, mpunga ndi chinangwa.  

Nthaka inali yachonde pano yaguga. Kumboyoku anthu amalima osagwiritsira ntchito  fetereza koma panopa sakuteronso.  

Mu Nyanja ya Mthambithabi munali nsomba zokoma monga nthachi, nkhututu, mbununu,  chitemera ndi nkhalala koma panopa kulibe 

Kudambo la Mthabithabi kunkamera therere la kazirira.  

Mu nkhalango munali zipatso zokoma ndinso zopatsa thanzi monga kapwati, masuku,  nziru, kankhande, maye, nthudza, bwemba, mapoza ndi kasokolowe.  

Nthawi yadzinja m’nkhalangomu ankazula bowa wokoma kwambiri monga chifisi,  manyame, katerera, mnofuwankhuku ndi nkhwayukwayu.  

M’mudzimo munali mitengo yamankhwala amakolo monga mvunguti, msolo, kamphoni,  msambamfumu, mwavi ndi thundu. Mitengo ina ndi monga m’bawa, mlombwa,  mng’wenya, mgwalangwa, msopa, mkongomwa ndi mkalati. Anthu maliza chifukwa  chotcha makala ndi kusema ziboliboli 

M’nkhalango yam’mudzimo munalinso nyama monga akalulu, agwape ndi ntchenzi. 

Zinthu zonse zidatha pazifukwa izi:  

Nkhuli (kukonda kudya zankhuli)  

Kuotcha makala  

Kucheka matabwa ndi kusema ziboliboli  

Zotsatira zamchitidwewu ndi izi:  

Kusintha kwa nyengo  

Mvula ikugwa mwanjomba  

Ngozi zachilengedwe zidachuluka m’mudzimo  

Mlangizi wamkulu, Gogo Tsinde, adakumbutsa anthu onse kuti mfundo pa zoyenera kuchita  zikakambidwa m’malimana ndipo adzakumananso Loweruka pakatha sabata ziwiri ndipo  kuti limana lililonse lidzafotokozera bwalo mfundo zake.  

Asanadzutse Bambo Lungu, amfumu adayitanitsa gulu lovina la amayi ndi atsikana kuti  ayimbe komanso avine nyimbo imodzi yokamba za kuonongeka kwa chilengedwe komanso  kusintha kwa nyengo.  

BAMBO LUNGU 

Nkhanza kwa amayi ndi ana aakazi: Ndunayi idayankhula motere: 

Nkhani zokhudza nkhanza zomwe ankangomva ngati nkhambakamwa chabe zidayamba  kuchitika m’mudzimo.  

A Chiphiri amenya mkazi wawo koma ali woyembekezera chifukwa chobwera mochedwa  kuchokera ku nkhuni. Mapeto ake mkazi wake apita pa dera. Panopa a Chiphiri akugwira  ntchito ya kalavulagaga ku ndende. Bwanji iwo kuti azikatheba okha nkhuni! 

Amuna ambiri akagulitsa tsabola amalowerera ku Dwangwa. Amakaononga ndalama ndi  akazi oyendayenda. Zikatha ndalamazo mpamene amabwerako. Ku Dwangwa amabwerako  alibe kalikonse komanso atatenga matenda opatsirana pogonana.  

Akazi akuvutistidwa kuti azilima koma odyerera ndi ena. Akatenga mnatenda amavutitsa  akazi awo powasamala komanso umasiye 

Anthu ambiri ofunikira m’mudzimu, anali atamwalira ndi matenda a edzi.  Bambo Pedegu adamangidwa kamba ka kugwirira mwana wawo wompeza wazaka khumi.  Pasukulu yomwe adayandikana nayo padali aphunzitsi ena aamuna omwe ankafunsira tiana  tatikazi.  

Adapempha malimana kuti akaunikire mozama zedi nkhani ya amayi ndi atsikana  Adatsindika kuti mchitidwe wankhanza utha chaka chimenecho.  

Pasanalowe mayi Amuli ndi nkhani zina ziwiri, amfumu adayitanitsa gulu lovina la abambo  komanso la anyamata la Kanada kuti avine nyimbo imodzi yomwe imakamba za kuipa kwa  nkhanza kwa amayi ndi ana.  

MAYI AMULI 

Ndunayi idayankhula nkhani zitatu zokhuza achinyamata motere:  

  1. a) Makhalidwe a anyamata ndi atsikana  

Kale anthu ankati achinyamata ndi atsogoleri amawa.  

Makono amati achinyamata ndi atsogoleri alero komanso amawa popeza: 

Makono ali m’maudindo ndipo akutsogolera pa zochitika zosiyanasiyana. 

Adakali anthete ndipo ali ndi zaka zingapo kutsogolo; dziko lidzakhalabe m’manja  mwawo. Makolo monga iwowo adatsala pang’ono kumwalira.  

Akadzamwalira, achinyamata adzasunge mawu awo.  

Anyamata ambiri m’mudzimo adalowerera komanso adasochera:  

Amangokhalira kumwa mowa ndi mankhwala ozunguza bongo. Ambiri mitu yawo  sinkayenda bwino.  

Ena akumakhwewa chamba. Mapeto ake akumapenga nanamizira nkhalamba kuti  zawaloza.  

Atsikana sankavala bwino m’mudzimu: Ankavala kazimoto/ndekesha (zovala  zazifupi kwambiri) pamaliro nkumakanika kukhala pansi.  

Atsikana amayenda bere lili pamtunda ngati logulitsa.  

Achinyamata analibe chidwi ndi makhalidwe abwino amakolo  

Miyambo yakale yoipa idathetsedwa.  

  1. b) Achinyamata ndi ndale 

Achinyamata amatengeka ndi zandale, makamaka nthawi yamisonkhano yokopa anthu.  Akasuta chamba komanso akamwa kachasu, amayambitsa chipolowe.  Zipolowe zomwe adachita tsiku lina zidaphetsa anzawo ophunzira bwino ndipo makolo  awo anali kusowa mtengo wogwira kamba ka imfa yawo.  

Ana a atsogoleri azipani sachita nawo zipolowe ndipo amakhla otanganidwa ndi  maphunziro kuti nawonso adzawalamulire.  

  1. c) Kusalana  

Anthu ena anali kusalidwa pazochitika za m’mudzimo kamba ka kuti ndi amtundu wina  kapena chimbedzo china.  

Anthu ankasalidwa pantchito monga kulima msewu, zomwe amalandirapo ndalama  komanso pa zinthu zaulere monga kulandira chakudya chomwe mabungwe apereka kwa  anthu ovutika.  

Mayiwa adafotokoza ndi chitsanzo kuti mwana akabadwa kuchipatala onena uthenga  samati kwabadwa Mkhirisitu, Msilamu, Mkunja Kapena Mchewa, Myawo ndi Mlomwe  kapena Mtumbuka. Chimodzi wopereka uthenga wamaliro sasiyanitsa.  

Sukulu yamm’udzimo inali yampingo koma ophunzira ake anali amipingo  yosiyanasiyana osati mpingo wa eni sukuluwo. Aphunzitsinso anali amipingo  yosiyanasiyana. Chimodzimodzi, chipatala cham’mudzimo chinali champingo koma  ogwira ntchito ndi olandira thandizo anali amipingo yosiyanasiyana.  

Anthu amipingo ndi mitundu yosiyana amadalirana; n’chifukwa chake akuyenera  kukhalira limodzi komanso kugwira ntchito limodzi. 

Anthu amene amalimbikitsa za sankho ndi opanda nzeru komanso osaganiza mozama. 

MAWU A MFUMU 

Amfumu adauza gulu lonse kuti mfundo zomwe zinalipo zinali zokhazo ndipo  adapempha Gogo Tsinde kuti awakumbutse anthu mfundo zomwe zidakambidwa  pamsonkhanowo. Gogo Tsinde adawuza Mayi Mwenda omwe adafotokoza mwachidule  mfundo zamsonkhano. Pambuyo pa zonse panali chidyerano.  

Aliyense amadya chakudya chomwe adatenga pamodzi ndi anthu ena osati abale ndi  anansi ake. Gogo Tsinde adakumbutsa anthu kuti akatsiriza kudya apite m’malumana  mwawo kuti agwirizane tsiku loti akumane ndipo akambirane zomwe adamva  pamsonkhanowo.  

Pavuto lililonse apeze magwero osachepera atatu komanso akambirane momwe  angalithetsere vutolo. Nduna zamfumu zidzayendera malimana kuti zione m’mene zinthu  zikuyendera. Mfumu Tandwe idatseka zonse pokumbutsa anthu kuti adzakumananso  Loweruka pakapita sabata ziwiri ndipo lumana lomwe silidzapezeka lidzapereka mbuzi  imodzi. 

ZIPANGIZO  

  1. Zining’a

Kuchita kaliunji: Kukumana 

Tigundane mitu: Kukambirana mokuya 

Waziwala m’maso: Wamisala 

Amvula zakale: Akale 

Anagonera dzanja: adamwalira 

Anadula phazi: Anasiya kubwera pamalo 

Zooneka ndi maso: Zodziwika bwino 

Ikugwa mwanjomba: Ikugwa yochepa komanso mwa apo ndi apo Taima mitu: Tadabwa kwambiri 

Anapita padera: Adabereka mwana wakufa. 

Kukhalira m’mphanthi: Kukhala movutika komanso mwamantha kwambiri Mwabwerako manja ali m’khosi: Mwabwerako opanda chilichonse Adatsikira kumsitu: Adamwalira 

Dzuwa latsala pang’ono kutilowera: Tatsala pang’ono kumwalira. Kumbiya zodooka: Kumanda 

Kukhwewa: Kusuta  

Zikutidulitsa mutu wazizwa: Zikutidabwitsa  

Kuzitengera pamgong’o: Kuchita zinthu mosazimvetsa bwino komanso mopitiriza  muyeso  

Zoyika moyo pachiswe: Zoti zikhoza kuononga moyo  

Ukadziwotche: Kulimba mtima kololera ngakhale kufa  

Mutayabwidwa ndi chitedze: Mutatenga matenda opatsirana pogonana. 

2. Mikuluwiko  

Chala chimodzi sichiswa nsabwe./Mutu umodzi susenza denga: Munthu sangachite  zinthu yekha; amathandizana ndi ena.  

Mawu a akulu akoma akagonera: Mawu a akulu amadzapherezera pakapita nthawi. 

3. Mvekero  

Mbalambanda: kuonekera  

Mbwandawumbwandawu: kuyenda motopa  

MAPHUNZIRO 

  1. Nkhanza  

A Chiphiri adalekerera mkazi wawo woyembekezera ndipo ali wolema kuti akatole  nkhuni kudondo.  

A Chiphiri adamenya mkazi wawoyu pamene adabwera mochedwa kuchokera  kunkhuniku.  

Bambo Pedegu adagwirira mwana womupeza wazaka khumi.  

Azibambo akagulitsa tsabola, amapita ku Dwangwa kukasakaza ndalama ndi akazi  oyendayenda chonsecho ankalima ndi akazi awo  

Mamuna wina adafuna kugwirira mayi ake omubereka. 

  1. Mudzi wa mfumu Tandwe unali wadongosolo  

Mfumu Tandwe simagwira ntchito yokha. Idagawira nduna zake zochita ndipo nduna  iliyonse imagwira ntchito yake molumikizana ndi akuluakulu a m’malimana.  Pamsonkhano, aliyense amatsatira ndondomeko yamalonje poyankhula.  

  1. Chikondi  

Mayi Pedegu adapita kukawazonda amuna awo kundende ngakhale adamangidwa kamba  kogwirira mwana wawo womupeza.  

Atsogoleri m’mudzi mwa Mfumu Tandwe adathetsa miyambo yakale yamokolo yoyipa  monga kulowa kufa, chokolo komanso kupondereza azimayi.  

  1. Kusunga chinsinsi  

Azimayi ena amabisa amuna awo akagwirira ana aakazi. 

  1. Mchitidwe wosasiyanitsa amuna ndi akazi (gender) 

Mfumu Tandwe idali ndi nduna zazimuna komanso zazikazi ndipo mlangizi wamkulu ndi  ena oyendetsa zinthu panthawi yamsonkhano adali akazi. 

  1. Kuganiza molakwika 

Makolo a anyamata omwe adapenga ndi chamba ankati anyamatawo adalodzedwa ndi  nkhalamba. 

  1. Kusasalana 

Anthu a m’mudzi mwa Tandwe, omwe anali osiyana zipembedzo ndi mitundu yomwe  ankapita ku sukulu ndi chipatala cha mpingo ngakhale kuti zinthu ziwirizi zinali za  mpingo wosiyana ndi anthuwo. 

  1. Kulowerera 

Achinyamata a m’mudzi mwa mfumu Tandwe anali osokonekera m’njira zosiyanasiyana.

9. Kusasamala 

Anthu a m’mudzi mwa Tandwe adadula mitengo pocheka matabwa, kuotcha makala  komanso kusema ziboliboli. Mitengo yambiri idatha. Izi zinadzetsa mavuto a  zachilengedwe mu mudzimo 

Anthu ankawedza nsomba mwadyera choncho zambiri zidatha 

  1. Kuganiza mwakuya 

Amfumu amayitanitsa gulu la ovina monga amayi ndi atsikana komanso abambo ndi  anyamata a Kanada pambuyo pa zoyankhula za nduna. Izi zimathandizira kuti anthu  asatope komanso asanyinyirike kutalika kwa msonkhano. Izinso zimapereka mpata kwa  woyankhula kuti akonzekere.

error: Content is protected !!
Scroll to Top