NUNSU YOYAMBA
Ku bwalo la masewero: Kaziputa anyoza Chamdothe
∙ Kaziputa adakumana ndi Chamdothe pabwalo lazamasewero ndipo adamunyoza kuti ndi opusa ndi anzake onse popeza
✔ ankachita masewero omvetsa chisoni.
✔ amayimba nyimbo zomvetsa chisoni pamene anthu ena onse anali kusangala. ✔ amadziyerekeza ndi birimankhwe wobwretsa imfa.
✔ anthu ochenjera sachita masewero okamba za imfa.
∙ Kaziputa adapeperetsa Chamdothe pomuuza kuti atafune khala n’kunena kuti ngochenjera ndipo akatero adzasiya kumunena kuti chidzete. Chamdothe adatsomphola khalalo n’kulitafuna koma adatsamwa nalo. Kaziputa adaonjezera mnyozo wake pomunyodola Chamdothe kuti anthu ochenjera sadya makala. Chamdothi adakwiya mwakuti pamene Kaziputa amachoka pabwalo adamutsatira ngakhale Dama ankamuletsa.
∙ Kumbutso: Chamdothe adauza Kaziputa kuti gulu lawo limaonetsa chisangalalo poyimba nyimbo zachisoni choncho kuyimba nyimbo zachisoni sikudali kupusa.
∙ Kunja kudayamba mabingu ndi ziphaliwali ndipo Dama adauza anzake kuti mvula idayenera kugwa panthawiyi. Chamdothe, pozindikira mavuto ake monga mwana wadongo, adayamba kuthawira kwawo. Panthawiyi, mayi ake a Chamdothi ankamuyitana ndi nyimbo ya “Chamdothe thawa mvula.” Zione adamunyengerera Chamdothe kuti asapite kwawo popeza anali kusewerabe.
∙ Chamdothe atafika kunyumba adafuna kudziwa kuchokera kwa amayi ake kuopsa kwa kuvumbidwa ndi mvula. Ndatopa, mayi ake, adamufotokozera kuti iye anali wosiyana ndi anthu enawo popeza adachita kuombedwa ndi dongo choncho sakuyenera kukhudzidwa ndi dontho lamvula: angadzabwerere ku dongo komwe iye adachokera. Iye adali ndithu mdani wamvula yomwe idali imfa yake.
MFUNDO ZIKULUZIKULU
- Chikondi/Chilungamo/Kuteteza
∙ Ndatopa adamuuza mwana wake Chamdothi kuti adapangidwa kuchokera ku dongo choncho adayenera kumathawa mvula yomwe ikadatha kumupha.
∙ Mayiyu adafotokozera mwana wake momveka bwino za umoyo wake ndipo tsiku lina ataona kuti kunja kwayamba mabingu ndi ziphaliwali adayamba kumuyimbira kanyimbo komuyitanira kunyumba kuti tsoka lisampeze popeza mwana adali yekhayo.
2. Chidwi
∙ Chamdothe adafuna kudziwa chomwe mayi ake ankaopa pomuyitana ndi nyimbo kuti athawe mvula.
- Kunyoza
∙ Kaziputa adanyoza Chamdothe ndi anzake kuti anali opusa poeza amayimba nyimbo zomvetsa chisoni pamene ena onse ankasangalala.
- Ulemu
∙ Chamdothe adavomera kuyitana kwa amayi ake ndipo adapita mwachangu ngakhale Zione ankamunyengerera kuti anali kusewerabe.
- Nkhanza
∙ Kaziputa auza Chamdothe kuti adye khala kuti awonetse kuti ndi wochenjera. Chamdothe adya ndipo atsamwa. Kaziputa amuseka
∙ Kaziputa akankhira Chamdothe pansi nagwa pomwe iye amayerekeza kuyenda kayendedwe ka birimankhwe. Pamene akuyesera kuti adzuke, gulu la Kaziputa limukanikizira pansi ndipo Kaziputa amuopseza Chamdothe.
NUNSU YACHIWIRI
Kunyumba kwa Ndatopa: Kubadwa kwa Chamdothe
∙ Ndatopa adaloleza Chamdothe kuti apite akasewere ndi anzake. Ndipo pambuyo pake Mayi Lunda adabwera kudzacheza ndi mayi a Chamdothe. Mayiwa adampeza mnzawoyo ali m’malingaliro ndipo atamufunsa adati ankakumbukira ubwana wawo.
∙ Azimayi awiriwa adavinira limodzi gule wa bongololo ndipo Mayi Lunda adanyamuka n’kumapita. Ndatopa adakumbukira mkangano womwe udachitika ndi mamuna wake Angozo pankhani yakusowa mwana ndipo udachititsa kuti mamunayo asamuke pakhomo. Ndatopa adakumbukira zinthu zotsatirazi:
✔ Angozo adamutcha Ndatopa buthu popeza adalibe mwana.
✔ Abale a Angozo ankamufunsa mafunso ambirimbiri ndipo asuweni ake aakazi ankamunena kuti adangodzivutitsa kupeza mkazi.
✔ Angozo ankati anzake ankamunena kuti Kalulu adamudutsa m’mphechepeche. ✔ Ndatopa adauza Angozo mamuna wake kuti ankamwabe mankhwala omwe awiriwa adakatenga kwa ng’anga ina.
✔ Angozo ankafuna kutenga mkazi wina kuti amuberekere ana.
✔ Angozo adamulowola Ndatopa kwa Asena.
∙ Mkangano umenewu udachititsa Ndatopa kuganiza zongoomba chidole ndi dongo ndipo adakatapadi dongolo nadzitsekera m’nyumba mwakuti pamene Mayi Lunda adabwera kudzacheza, sadatsekule chitseko. Adamunamiza mnzawoyo kuti anali kumva mutu koma pomumvetsa Ndatopa, Mayi Lunda adamuuza kuti amuna amalemekeza mkazi akawaberekera ana ndipo kuti ngati mkazi satero amakhala wopanda pake. ∙ Ngakhale mayiyu adayesetsa kunyengerera Ndatopa kuti amutsekulire aone mbiya yomwe amaomba, iye sadatsekule. Ndatopa adauza Mayi Lunda kuti awayitana akatsiriza kuomba mbiyayo popeza anali atangoyamba kumene ntchitoyo.
∙ Panthawiyi Ndatopa akusisima adaomba chidole ndipo adapempha Chiuta kuti ampatse mwana. Adatsinzina nakweza manja kumwamba kwa Mulungu ndipo chidolecho chidakhala ndi moyo. Mayi Lunda ankadikirabe panja panyumbayo koma Ndatopa adawauza kuti anali asadatsirizebe kuomba ngakhale mphika umodzi.
∙ Chamdothe, mwana yemwe anali atangoombedwa chakumene ndipo adapatsidwa moyo, adayamba kuyankhula pofunsa za mayi yemwe anali kunja kwa nyumbayo koma mayi ake adam’phimba pakamwa kuti Mayi Lunda asamumve. Pambuyo pake Ndatopa adauza Mayi Lunda kuti awapititsira kwawo miphika yomwe anali atangotsiriza kumene kuomba ndipo ayinyamula mosamala.
∙ Kumbutso: Mayi Lunda ndi omwe adaphunzitsa Ndatopa kulotcha mimphika.
Chamdothe pabwalo tsiku loyamba
✔ Kaziputa adafuna kuti amudziwe Chamdothe ndipo adazizwa atamva kuti ndi mwana wa Ndatopa popeza adauzidwa kuti Ndatopa sakadakhala ndi mwana ndiponso analibe mwamuna.
✔ Puna adaonjeza kuti Ndatopa akadakhala ndi mwana sakadakula anthu osadziwa.
✔ Chamdothe adauza Kaziputa kuti amake adamtenga kubanja lina m’mudzi wa Kuserikumvenji.
✔ Puna ndi Kaziputa sadakhulupirire ndipo adayamba kumukankha Chamdothe kuti anene zoona koma Lunda ndi Zione adaleretsa. Lunda adaopseza Kaziputa ndipo Chamdothe adapeza mwayi wothawira kwa amayi ake.
Chamdothe ndi amayi ake
∙ Chamdothe adafotokozera mayi ake zomwe ankanena Kaziputa ndi Puna kuti iwo alibe mwana komanso mudzi wa Kuserikumvenji kulibe.
∙ Ndatopa adachenjeza Chamdothe kuti asamawayandikire anthu awiriwa angadzamuphetse. Adamuuzanso kuti asamale ndi Kaziputa popeza anali ndi mavuvu ndipo Ndatopa sakadatha kumuteteza kumavuvuwo.
∙ Ngakhale Chamdothi adanena kuti ankafuna kukhala ngati mnyamata wina aliyense pophunzira mavuvu n’kuwagonjetsa popeza mamuna aliyense amatero kuti akule, Ndatopa adamuuza kuti sanayenera kuchita masewero onyansawo kuti akule.
∙ Chamdothe adauza amakewo kuti Zione, Dama ndi Lunda adamulandira kale ngati mnzawo kubwalo. Ndatopa adamuchenjeza kuti anzakewo asamupititse koopsa.
∙ Chamdothe agwa m’chikondi ndi Zione
✔ Adakangana ndi Kaziputa popeza ankati Zione ndi wake (mkazi wa Kaziputa) ndipo adamutsimikizira kuti tsopano ndi mkazi wake (wa Chamdotheyo).
✔ Adalandira chibangiri kuchokera kwa Zione.
Matanthauzo amawu
- a) Mavuvu : Khalidwe lochita zinthu mosaugwira mtima, modzionetsera komanso moonjeza. b) Gwetseranani mumchenga: Siyani kukangana ndipo yanjanani.
- c) Chibangiri: Khoza lachitsulo lovala kumanja
- d) Chamdothi: Mwana wochita kuumbidwa kuchokera ku dongo
- e) Kaziputa: Mnyamata wokonda kuputa dala ndikunyoza Chamdothe.
- f) Ndatopa: Mayi wolema chifukwa chosakhala ndi mwana nkumavutana ndi mamuna wake, g) Zione: Ona zinthu monga zabwino ndi zoyipa zomwe
MFUNDO ZIKULUZIKULU
- Nkhanza
∙ Kaziputa ndi Puna adayamba kumukankhizirana Chamdothe pamene ankamutsutsa zoti sadatengedwe ku banja lina ndipo mudzi wotchedwa Kuserikumvenji kudalibe.
2. Kuteteza
∙ Zione ndi Dama komanso Lunda adamuleretsa Chamdothe pomuuza Kaziputa kuti iye amangodana ndi Chamdothe ndipo adaonjezanso kuti asayerekeze kumuvutitsa Chamdothe.
∙ Adamuopsezanso kuti mavuvu akewo asachitire munthu wam’mudzimo popeza akatero adzathesemulidwa.
- Chikondi
∙ Chamdothe ndi Zione adagwa mchikondi moti Zione adapereka chibangiri kwa Chamdothe.
∙ Chamdothe adauza Kaziputa, ngakhale anali wamavuvu, kuti Zione ndi mkazi wake. 4. Kukanika kulongosola
∙ Kaziputa adakanika kumufotokozera Chamdothe pamene adafuna kudziwa ngati iyeyo (Kaziputa) anali kuonetsera chikondi chake pa Zione pamene adanena kuti ndi mkazi wake.
- Bodza.
∙ Chamdothe anamiza Kaziputa kuti iye anachokera ku mudzi wa Kuserikumvenji. ∙ Ndatopa anamiza anzawo, Mayi Lunda kuti akuumba mbiya pomwe akuumba Chamdothe
NUNSU YACHITATU
Chamdothe kumtsinje
∙ Chamdothe adaomba mbuzi yadongo n’kumasewera nayo. Kaziputa adamulanda mbuziyo ndipo adapita nayo pamwala womwe unali pakati pa dziwe. Kaziputa adauza
Chamdothe kuti ankafuna kuona ngati Chamdothe angapulumutse mbuziyo. Adayigumula nayiponyera m’madzi.
∙ Zione ndi anzake ena adamuthamangira Chamdothe yemwe panthawiyi ankayenda m’mbali mwa mtsinje posafuna kuti alumphire m’madzi. Zione adauza Chamdothe kuti Kaziputa adachitira dala kugumula komanso kuponya m’madzi mbuzi yake pofuna kulipsira zomwe Chamdothe adachitira Puna usiku wina.
∙ Zione adakumbutsa Chamdothe kuti Kaziputa amachitira anzake zoipa ngakhale asadamuyambe. Kaziputa adakana Puna ku Mnjiri. Pochoka kumtsinjeku, Zione adampatsa Chamdothe nkhanu kuti akapereke kwa amayi ake popeza adakhala nthawi asadazilawe.
∙ Pochoka pamalopa Chamdothe adaganizira zinthu ziwiri zotsatirazi:
✔ Chomwe chinkamuchititsa Kaziputa kuti azimusungira nkhwidzi nthawi zonse
✔ Adalakalaka Zione atadzakhala mkazi wake
Chamdothe Kumunda
∙ Chamdothe adauza amake kuti adaganiza zopita nawo kumunda popeza sankafunanso kusewera panthawiyi. Ndatopa adafuna kudziwa kuchokera Chamdothe chomwe Zione adalinga popereka nkhanu kwa Chamdothe.
∙ Mwanayu adayankha amakewo kuti Zione adati nkhanuzo ndi zawo (za amakewo) osati za iyeyo. Mafunso omwe Chamdothe adaponyera Ndatopa adasonyeza kuti iye (Chamdothe) adagwa m’chikondi ndi Zione ngakhale kuti sadam’tchule dzina.
∙ Adakacheza choncho, Ndatopa adagwira nkhumbu yomwe panthawiyi inkapereka zinthu ziwiri: chakudya chokoma komanso macherechete.
∙ Pamundapa, Chamdothi ndi mayi ake, Ndatopa adacheza motere:
✔ Ndatopa adakana kumuuza Chamdothi nyimbo ya macherechete komanso ya nkhumbu.
✔ Ndatopa adauza Chamdothe kuti akadatha kugonetsa nkhumbu m’kakhola ndi kuyimba nyimbo yekha.
✔ Chamdothe adayankha kuti kutero ndi kuchitira nkhanza tizilombo monga nkhumbuzo.
Ndatopa adatsimikizira Chamdothe kuti nkhumbu zidalengedwa kuti zizidyedwa. ✔ Ndatopa adadziwitsa mwana wakeyo kuti anthunso adzafa ndipo uthenga wa imfa
udabwera ndi namzikambe kuchokera kwa Chiuta kupita kwa Mchewa kapena Mmaravi wamamuna ndi wamkazi pa Kapirimtiwa koma Chamdothe adayankha kuti nkhumbu/chilule siziyenera kuphedwa kamba ka uthenga wa imfa womwe udabwera ndi namzikambe popeza ndi tizilombo tating’ono ndipo imfa yake njopanda pake.
✔ Ndatopa adauza Chamdothe kuti imfa zisankha ndipo sifotokoza chifukwa chake. ∙ Asanatsirize macheza pamundapa kudamveka mkokomo wamvula kotero Ndatopa adamutenga Chamdothe nkuthawira naye kunyumba kuti asanyowe. Adasiya makasu ndi dengu.
MFUNDO ZIKULUZIKULU
- Chikondi
∙ Ndatopa adacheza ndi mwana wake ndipo adamufotokozera chiyambi cha imfa komanso adamuuzako za nkhumbu nampangira macherechete.
∙ Zione adapereka nkhanu kwa Chamdothe kuti akawapatse mayi ake popeza adakhala nthawi yayitali asadazilawe.
∙ Zione adamuthamangira Chamdothe, pamene adamuona akuyenda m’mbali mwa mtsinje, kuti asagwere m’madzi.
- Kuteteza
∙ Zione adamuthamangira Chamdothe, pamene adamuona akuyenda m’mbali mwa mtsinje, kuti asagwere m’madzi.
∙ Ndatopa adalolera kusiya makasu ndi dengu pamunda pofuna kupulumutsa Chamdothe ku mvula yomwe ikadamupha.
- Nkhanza
∙ Kaziputa abonthola mbuzi yomwe Chamdothe anaiumba. Apa anali ku mtsinje pomwe amasewera.
- Luso
∙ Luso loimba: Ndatopa ayimba nyimbo mpaka nkhumbu yomwe ikuluka kutera. Ndatopa aimbira nyima chelule mpaka kumugonetsa. Kenako amugwira
∙ Luso loumba: Chamdothe aumba mbuzi ku mtsinje. Ndatopa aumba Chamdothe.
Matanthauzo a mawu
∙ Nkhumbu: Kachirombo kooneka moyerera komwe kamakhala ndi mapiko olimba ndipo anthu amapangira mangwere.
∙ Macherechete: Choyimbira chopangidwa ndi chingwe chachitali chomwe anthu amatungirako mapiko a nkhumbu akunja navala m’khosi mokupatira, kenaka namayimba ndi zala.
NUNSU YACHISANU
Imfa ya Chamdothe
∙ Zione adapita kwa mayi a Chamdothe ndipo adawapempha kuti amutenge akasewere naye. Mayi a Chamdothe adamukaniza pomuuza kuti samafuna zoti mwana wawo Chamdothe akasewere kutali popeza nyengo yamvula inali itafika. Zione adalonjeza kuti akamudyetsa komanso akamusamalira bwino Chamdothe. Ndatopa adamuloleza Zione kuti amutenge Chamdothe.
∙ Zione ndi Chamdothe atafika pabwalo posewerera, Kaziputa adasiya Puna nanyamuka kuti akamukankhe Chamdothe koma Dama ndi Lunda adaleretsa. Mkangano wolimbirana Zione udabukanso pakati pa Chamdothe ndi Kaziputa motere:
✔ Chamdothe adauza Kaziputa kuti adali kale ndi Puna choncho anayenera kukhala ndi Punayo basi.
✔ Chamdothe adaonjezanso kuti n’kutheka kuti Kaziputa anali woyipa n’chifukwa chake Zione adasankha Chamdotheyo.
✔ Kaziputa adamuuza Chamdothe kuti sakhalitsa naye Zione.
✔ Kaziputa adamuuzanso mnzakeyu kuti Zione ndi mtsikana wokongola choncho sangakhale mkazi wa Chamdothe.
∙ Dama adalowerera mkanganowu ndipo adauza Chamdothe ndi Kaziputa kuti sadayenera kukanganirana Zione popeza awa adali masewera chabe (zamasanje). Zikadakhala zenizeni, makolo sakadawaloleza kuti azisowa kwa kanthawi.
∙ Kaziputa adamuyankha Dama kuti mudali zambiri m’masanje zoposa kungosewera za amayi ndi abambo.
∙ Macheza otsiriza a Chamdothe ndi Zione
✔ Zione adafuna kudziwa chomwe chidamuchititsa Chamdothe kuti amusankhe kukhala mkazi wake. Chamdothe adamuyankha kuti mwina ndi maphikidwe ake abwino abowa komanso adalawa nkhanu zake.
✔ Zione adatsutsa ganizoli ponena kuti nkhanuzo adaphika sanali iyeyo.
✔ Zione adafuna kudziwa ngati Chamdothe adawauza mayi ake za chibangiri chomwe Zioneyo adamupatsa koma Chamdothi adati sadwauze amake popeza ankasowa poyambira. Nkhaniyi idakwiririka ndi nkhani inzake yokhudza kaliyoliyo yomwe Zione ankati amuuzabe Chamdothe panthawi yopuma.
✔ Kunja kudamveka mabingu ndipo Chamdothe adatsanzika Zione kuti azipita koma Zione adamuuza kuti anali asadayimbe chimbo yotsekera masanje .
✔ Zione adamuuza Chamdothe kuti abisala m’nyumba yamasamba koma iye adamuyankha kuti nyumba yamasambayo singamuteteze.
∙ Mayi a Chamdothe, Ndatopa, adayamba kumuyitana kudzera m’nyimbo ya “Chamdothe thawa mvula.” Zione adathamanga ndi Chamdothe kuti akamusiye kwawo koma mnyamatayu adayamba kuwolowa n’kumachoka chiwalo chimodzichimodzi mpaka udatsala mutu wokha womwe udagwera pansi pamene Zione amawupereka kwa Ndatopa.
MFUNDO ZIKULUZIKULU
1) Kusasamala: Zione ankadziwa kuti Chamdothe sayenera kukhudza madzi kuopa kufa nawo koma adalolera kumuchedwetsa mpaka kumunywesa ndi mvula ndipo imfa yake idali yomweyo.
2) Kudziyenereza: Kaziputa adauza Chamdothe kuti Zione anali mkazi wokongola wosayenera kukhala mkazi wa Chamdothe koma iyeyo.
3) Kudziteteza: Chamdothe atamva mabingu adadziwa kuti mdani wake, mvula, wayandikira ndipo adatsanzika Zione kuti azipita kwawo ndipo pamene Zione adamuuza kuti akabisala panyumba yamasamba, Chamdothe adamuyankha kuti nyumba yamasamba singamuteteze ku mvula.
4) Kukwaniritsa lonjezo: Zione atenge mutu Chamdothe pomwe anasungunuka ndi mvula nakaupereka kwa amayi ake, Ndatopo. Umu ndi momwe adawalonjezera
Mawu ena ofunika kuwaunikira
- Chamdothe ankakhala moyo wosasangalala kwenikweni
∙ Nthawi zambiri ankavutitsidwa komanso kunyozedwa ndi Kaziputa. ∙ Iye ankakhala mwa mantha makamaka poganizira kuti mdani wake wamkulu ndi madzi. ∙ Kaziputa atamutengera mbuzi yake yadongo n’kupita nayo pamwala pakati pa mtsinje
iye adamulondola koma ankayenda m’mbali mwa mtsinje poopa kuti anganyowe ndipo anzake adamuthamangira nkumugwira kuti asalumphire m’madzi.
∙ Kunja kukaonetsa zizindikiro zoti mvula igwa iye amathawira kwawo mvulayo isanayambe poopa kuti anganyowe n’kugumuka.
- Fisi ali ndi bwenzi
∙ Kaziputa anali munthu woyamba dala anzake komabe anali ndi bwenzi lake Puna amene amachita naye zinthu nthawi zambiri ndipo kumasewero amasanje anali mkazi wake. ∙ Ndatopa adanyozedwa ndi mamuna wake Angozo pamene sankabereka komabe Mayi a Lunda ankamumvetsa ndipo ankayesetsa kuti asamakhale ndi nkhawa.