Course Content
Kufunika kwa Zisudzo
Chisudzo ndi nkhani yochitika kapena yopeka yomwe imafotokoza zinthu mokhala ngati zikuchitika kumene.
0/2
MITU YONSE MNKHANIYI
0/1
Khoswe Wa Padenga
Kukamba za Bonzo, Goli, Khoswe, Anne ndi Jubeki
0/2
Mudzi Wa Mfumu Tandwe
Kuonongeka kwa zachilengedwe ndi mavuto ena
0/3
CHAMDOTHE NDI ZISUDZO ZINA

NUNSU YOYAMBA  

Mgezenge ndi Nagama kunyumba kwawo  

Mgezenge akudziyankhulira yekha ndipo adandaula zinthu izi:  

Miyendo inkamuphwanya ndipo inkatero kamba kakuti iye adakalamba. 

Miyendo yake imafunika kukhala m’mwamba.  

Akazi ena akamakula amavuta kwambiri. (Adayankhula izi popeza mkazi wake Nagama  adachedwetsa kubweretsa mpando woti apachikepo miyendo.) 

Madandaulo a Mgezenge pamene amakambirana ndi mkazi wake 

Mkazi wake, Nagama, adachedwetsa mpando woti ayikepo miyendo. 

Iye ankadwala kusowa chisamaliro. 

Kusowa chikondi ndi chisamaliro ndi matenda ndithu. 

Ulemu wochokera kwa mkazi wake umaperewera. (Amamutchula “amuna anga” m’malo  mwa dzina lake “Mgezenge” pomuyitana ngakhale amalidziwa bwino dzinali.) Mkazi wakeyo amamuyankhula ali chilili. 

Madandaulo a Nagama mkazi wa Mgezenge 

Adakumbutsa mamuna wake kuti iye anali kudwala mwakuti sankachitira dala kuchedwetsa  kampando kopachikapo miyendo. 

Mgezenge, mamuna wake, sankamulabadira. 

Kumutchula mwamuna wake “Mgezenge” ndi ulemu 

Zotumphuka pa zokambirana za Mgezenge ndi mkazi wake 

Mgezenge ankamuyankhula mkazi wake moopseza komanso mwaukali.

Mgezenge ankanyinyirika ndi kudwala kwa mkazi wake mwakuti adamuopseza kuti akwatira  mkazi wina popeza iye (mkaziyo) sanali kugwira ntchito zambiri. 

Ku mayiko ena monga ku Napal, Tibet, Sri Lanka ndi mbali zina za China, mkazi amatha  kukwatiwa ndi amuna angapo. Mitala yochita mkaziyi imatchedwa Poliyandire.

Banja la Mgezenge linali ndi zifuyo zambiri: ng’ombe zopitirira makumi asanu ndi awiri (70)  komanso mbuzi zana limodzi ndi makumi awiri kudza mphambu zisanu ndi zinayi (129).

Umboni woti pamafunika munthu wothandiza ntchito pakhomo pa mgezenge Zifuyo zinalibe mbusa choncho zinkaononga m’minda ya wanthu. 

Zifuyo zimafunika munthu woti apite nazo ku dipi. 

Golosale imafunika dongosolo labwino. 

Kumbutso 

Ngakhale pamafunika munthu woti athandize kugwira ntchito, monga kusamala ziweto  pakhomo pa Mgezenge, yankho la vutoli silinali kukwatira mkazi wina monga amanenera  Mgezenge. 

Pamene Nagama adauza mamuna wake Mgezenge kuti anali kuyankhula m’zining’a,  Mgezengeyo adalusa nakunga chibakera n’kumuponyera mkazi wakeyo koma iye adzinda  mwakuti Mgezenge adagwa pansi ndipo amaoneka kuti ankamva ululu kwambiri. 

Mgezenge ndi Zikani 

Zikani adautukira naodira kunyumba kwa Mgezenge panthawi yomwe Nagama adazinda  chibakera cha Mgezenge kachiwiri ndipo Mgezenge adagwa ngati chithumba.

Zikani adathandiza Mgezenge kuti adzuke ndipo Mgezenge adamukumbatira mosonyeza  chikondi. Izi zidachititsa Zikani kuti amukankhe Mgezenge ndipo adatsala pang’ono  kugwanso. 

Zikani atawafunsa alamu ake a Mgezenge kuti afotokoze chomwe chinachitika kuti apezeke  atagwa, Mgezenge adamuyankha kuti adaterereka pamene ankafuna kuti akhale pampando.

Mgezenge asirira momufuna Zikani Pamene Zikani adatsanzika nayamba kuyenda kuti  alondole mkulu wake Nagama kukhitchini, Mgezenge adadziyankhulira mawu otsatirawa  akumuyang’ana: “Mulungu sungamumvetse. Adalenga munthu wamkazi kuti akhale wothangatira  mamuna. Atamulenga mkaziyo, anapitiriza ndipo akupitiriza kumukongoletsa munthu wamkazi.  Atsikana akubadwa masiku ano akuposa amawo kukongola. Ndipo Mulungu amati akalenga mwana  wamkazi chaka chino, chaka chamawa amadzalenga njole yozunguza mutu. Atsikana amakono  akamayenda amakhala ngati akuvina ndipo akamayankhula amakhala ngati akuimba nyimbo  zanthetemya.”  

Zotumphuka pa mkumano wa Mgezenge ndi Mayamiko 

Mayamiko adali mwana wa a Mackson Chikoya ndipo anali ndi zaka khumi ndi ziwiri (12). Mgezenge adagwirizana ndi bambo a Mayamiko kuti awapititsire nkhuni koma mtengo  weniweni ndi kuchuluka kwa nkhuni (kukula kwa mtolo) sadagwirizane. Mayamiko  adadziwa kuti mtolowo wakwanira pamene bambo ake adavomera ndi mutu pamene iye  ankadutsa panyumba akupita kwa Mgezenge. 

Mayamiko ankachita malonda amakala. 

Mayamiko sadapite kusukulu popeza atate ake adamujombetsa kuti akasake nkhuni zomwe  adakapereka kwa Mgezenge komanso zovala zake zinali zokuda mwakuti ankayembekezera  kuti Mgezenge akampatsa ndalama zankhuni zomwe adapititsazo, akagule sopo wochapira  pobwerera kwawo. 

Golosale ya Mgezenge idali yotseka ndipo Mgezenge adapsa mtima nati amuchotsa ntchito  Funsani, mnyamata yemwe amagulitsa m’golosaleyi. 

Mgezenge amamukhulupirira Funsani. 

Zipangizo m’gawoli 

  1. Zifanifani 

Kumangoti amuna anga amuna anga muli pholi ngati mlongoti. 

Agwanso ngati chithumba. 

Osamathamangira kufunsa mafunso ngati aphunzitsi. 

Atsikana amakono akamayenda amakhala ngati akuvina 

Akamayankhula amakhala ngati akuimba nyimbo zanthetemya. 

  1. Msemphano 

Zikani atawafunsa alamu ake a Mgezenge kuti afotokoze chomwe chinachitika kuti  apezeke atagwa, Mgezenge adamuyankha kuti adaterereka pamene ankafuna kuti akhale  pampando. Zoona zake n’zakuti Mgezenge adagwa pamene mkazi wake Nagama  adazinda chibakera chomwe adamuponyera. 

  1. Mvekero  

Pholi: chiimirire  

MFUNDO ZIKULUZIKULU 

  1. a) Bodza  

Zikani atawafunsa alamu ake a Mgezenge kuti afotokoze chomwe chinachitika kuti  apezeke atagwa, Mgezenge adamuyankha kuti adaterereka pamene ankafuna kuti akhale  pampando.  

  1. b) Kusirira  

Mgezenge ankamusirira kwambiri Zikani mwakuti pamene ankamudzutsa atagwa  pamene Nagama adazinda chibakera chomwe adamuponyera, adamukumbatira  mosonyeza chikondi.  

  1. c) Kuyipa kwa kuononga chilengedwe  

M’mudzi m’mene ankakhala Mgezenge ndi anthu ena mitengo idatha ndipo idayamba  kusowa kamba ka m’chitidwe wootcha ndi kugulitsa makala. 

  1. d) Nkhanza  

Mgezenge adafuna kumenya mkazi wake pazifukwa zosakwanira.  

  1. e) Kukhulipirira wantchito  

Mgezenge adamusiyira Funsani makiyi akugolosale.  

  1. f) Kumvera makolo  

Bambo Chikoya adamujombetsa mwana wawo Mayamiko kuti akasake nkhuni ndipo  akazitule kwa Mgezenge. Mayamiko adajombadi nachita zomwe adauzidwa ndi atate  ake.  

  1. g) Kuganiza mosiyana  

Nagama ankamuyitana mamuna wake Mgezenge pomutchula kuti “amuna anga” ndipo  adaona kuti ankachita ulemu poteropo.  

Mgezenge sankasangalatsidwa ndi mchitidwewu ndipo adauza mkazi wakeyo kuti ndi  mwano kuti azimutchula “amuna anga” chonsecho dzina lake anali kulidziwa.  

NUNSU YACHIWIRI  

Zotumphuka pamacheza a Nagama ndi Zikani  

Nagama adadabwa kuti Zikani adafika kunyumba kwake panthawi yomwe anayenera  kupezeka m’kalasi kusukulu.  

Zikani adathangitsidwa kusukulu popeza sadapereke ndalama zochitira chitukuko pasukulu  (monga kumanga zimbudzi) komanso zogulira bukhu lomwe adataya.  

Bukhu lomwe Zikani anayenera kulipira lidasowa pamene iye adapita kukadzithandiza  kuchimbudzi.  

Pasukulu pomwe Zikani ankaphunzira pamafunikadi zimbudzi zoonjezera popeza ophunzira  ankakhala pamzere wautali nkumadikirana kuti alowe ku zimbudzi zomwe zinalipo. 

Nagama adandaula zinthu zotsatirazi malingana ndi kubedwa kwa bukhu la Zikani: 

Kuba ndi koipa m’dziko popeza kumachititsa kuti mwini katundu avutike. 

Anthu amene amakhala akuba pasukulu sasiya mwansanga.  

Anthu amene akuba makonowa adayamba m’chitidwewu adakali ana. 

Makolo a Zikani ankadalira banja la Nagama pankhani zachuma.  

Mkazi akalowa m’banja kamba ka umphawi, amakhalira kumulambira mamunayo.  Mgezenge akakwiya ndi chinthu, mkwiyo umathera pa mkazi wake Nagama. Nagama amakhala mwamantha ndi mamuna wake koma ankamumasukira mchemwali wake  Zikani.  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI  

  1. Kuba ndi koipa m’dziko popeza kumachititsa kuti mwini katundu avutike.  Wophunzira wina adaba bukhu la Zikani kotero kuti Zikani anayenera kulipira.  5. Kudalira  

Zikani adadalira makolo ake kuti amupatsa ndalama zochitira chitukuko pasukulu  komanso zolipirira bukhu lomwe adataya.  

Makolo a Zikani ankadalira kwambiri banja la Mgezenge ndi Nagama pankhani  zachuma.  

Zikani adadalira mnzake kuti amuyang’anira bukhu pamene iye adapita kukadzithandiza. 

6. Nkhanza  

Mgezenge chilichonse chikamuvuta, mkwiyo umadzathera pa mkazi wake. 

5. Kuba 

Zikani aberedwa buku lake kusukulu pomwe analisiya atapita ku chimbuzi  kukazithandiza 

Zipangizo  

  1. Mikuluwiko  

Wamva m’mimba ndiye atsekula kukhomo: Amene ali ndi vuto ndipo akufuna  chithandizo mwansanga, akuyenera kuchitapo kanthu.  

Wopempha safulumira: Wopempha amayendera maganizo a wopereka chithandizoyo. 

2. Msemphano  

Azimayi am’mudzi ankachitira nsanje Nagama ponena kuti adakwatiwa ndi mamuna  wolemera (adakwatiwa n’kumbuyo komwe). Azimayiwa sankadziwa kuti Mgezenge  anali mamuna wovuta mwakuti Nagama ankavutika ndipo amakhala moyo womulambira.  Chilichonse chikamuvuta, mkwiyo umadzathera pa mkazi wake.  

NUNSU YACHITATU  

Mgezenge ndi Funsani ku golosale  

Mgezenge adakwiya kwambiri popeza Funsani sanatsekule golosale ndipo pamene  adatulukira adamutchula kuti ndi wopusa.  

Funsani sadatsekule golosale chifukwa ankadwala ndipo adapita kukalandira thandizo  lamankhwala kuchipatala. Mgezenge sadamve izi: adangoti Funsani ndi wopusa komanso  waulesi.

Mgezenge adauza Funsani kuti achite sitoko patsikulo ngakhale kuti Funsaniyo sankadziwa  tanthauzo lake. 

Mgezenge adayankhula kuti makolo a Funsani ankagwira ntchito pa esiteti ya Mgezenge  koma adapititsidwa ku esiteti ya mnzake wa Mgezenge kutali. Pochoka iwo adavomereza  kuti Funsani atsale azigwira ntchito mgolosale ya Mgezenge. 

Ngakhale Funsani adamuuza Mgezenge kuti cholembera chomwe adachipeza m’thumba  mwake adachita kugula kuti azilembera, Mgezenge sadamumvere ndipo adamuchotsa ntchito  namuuza kuti malipiro ake ndi cholembera chomwe adatengacho. 

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI 

  1. Nkhanza 

Mgezenge adamulemba ntchito Funsani ngakhale adali mwana wazaka khumi ndi ziwiri  (12). 

Mgezenge adamunyoza Funsani pamene sadatsegule golosale kamba koti adapita  kuchipatala kukalandira thandizo lamankhwala pamene adadwala malungo. Mgezenge adachotsa ntchito Funsani popanda zifukwa zokwanira. 

Mgezenge adamukwenya pakhosi Funsani ndipo sadampatse malipiro pamene  adamuchotsa ntchito ponena kuti malipiro ake ndi cholembera chomwe chidapezeka  m’thumba lake. 

  1. Kukayikira/Kuganiza molakwika 

Mgezenge adauza Funsani kuti makolo ake povomereza zomusiya kuti azigwira ntchito  mugolosale ya Mgezenge adagwirizana zoti amubere. 

  1. Umphawi umachititsa munthu kuti aganize moperewera. 

Makolo a Funsani adavomereza zomusiya mwana wawo wazaka khumi ndi ziwiri kuti  azigwira ntchito m’golosale ya Mgezenge pamene iwo amatumizidwa kukagwira ntchito  kutali ku esiteti ya mnzake wa Mgezenge, zotsatira zake Mgezenge adamuchita nkhanza  mwanayo. Zipangizo 

Matanthauzo a mawu  

Malungo adandithyola mafupa: Malungo anandivuta zedi 

Ndipsi: wakuba 

Sitoko: Kuwerengera katundu yemwe watsala m’shopu pofuna kupeza katundu amene  watuluka ndi kufananitsa ndi ndalama zomwe zilipo katunduyo atagulitsidwa.  

NUNSU YACHINAYI 

Zotumphuka pa kucheza kwa Abiti ndi Gama kunyumba kwawo pambuyo pa msonkhano  wa kwa Agulupu 

Monga Mgezenge, naye Gama anali wosachedwa kupsa mtima ndipo mkazi  akamamuyankhula ali chilili amatanthauzira kuti ndi mwano. 

Mkazi wake, Abiti, atayankha kuti si amfumu amene adapereka chigamulo cha nkhani  yamunda iye adapinda chibakera namuloza nacho nkumuuzanso kuti safuna zopusa. Chitukuko chamsewu ndi chomwe chidautsa mapiri pachigwa.  

Amfumu (Agulupu Watison Kajiyanike Jere) adauza Gama kuti msewu udutsa m’munda  mwake ndipo “Road Reserve Boundary” imadyanso gawo lalikulu zedi lamundawo.  A Gulupu Watison Kajiyanike Jere ankaopedwa m’mudzi kamba ka zamatsenga zomwe  

adamuchita mlamu wawo (atawalakwira nkukana kupepesa, adangomutchula dzina ndipo iye  adachita khungu ali kutauni).  

Anthu m’mudzimu adaononga mitengo ndi malonda amakala.  

Agulupu adayankhula anthu mwamwano komabe adayankhula chilungamo.  

Mgezenge akumutula Nagama kwa makolo ake  

Adatulukira atamugwira padzanja ndipo adayankhula mwamwano ndi makolo a Nagamayo  kuti akudzamusiya koma a Gama adamuyankha mwaukali namuuza kuti akhale pansi popeza  sakadagona usiku ngati sakadathana naye masana atsikulo.  

Nagama adandaula kuti Mgezenge adamumenya usiku wonse.  

Mgezenge adapereka dandaulo lake kudzera m’zining’a ziwiri: mpando ndi mbalame.  (Munthu amene ali ndi mpando koma nkumagona pansi, mutu wake ndi wosakoka. Mbalame  yomwe ili ndi chisa koma ikuopa kugona poti muli njoka, singalimbe mtima kuti ilowemo  m’chisamo.) Apa Mgezenge amafuna kutanthauza kuti sakukhala pamodzi ndi mkazi wake  monga banja kamba ka zovuta zina zomwe kwa iye zinali zosakwanira.  

Zotumphuka pazokambiranazi  

Mgezenge ndi Gama anali amuna osachedwa kupsa mtima.  

Mkazi wa Gama, Abiti, amatsatira nkhani ndipo amamvetsa zinthu.  

Abiti ndi mamuna wake Gama ankakomedwa ndi chuma cha Mgezenge mwakuti sanali  kukonza mavuto a banja la mwana wawo Nagama moyenera. Iwo amalimbikira kumuuza  Nagama kuti sakufuna kuti awathawitsire mkamwini wabwinobwinoyo.  

Mgezenge ankamufuna kwambiri Zikani.  

Abiti ndi mamuna wake anali wokonzeka kumupereka mwana wawo Zikani kwa Mgezenge  kuti akhale mkazi wake wachiwiri n’cholinga choti apitirize kulandira ndalama zake.  

Zomwe zidachititsa Makolo a Nagama kuti achite Shazi/Mbirigha/Isakulwa/Nthena Nagama adakhala pafupifupi chaka chathunthu asakupeza bwino mwakuti Mgezenge sanali  kulowa m’nyumba.  

Samafuna kuti Mgezenge ayambe kuzemberana ndi akazi adera.  

Matenda a Nagama  

Amatsegula m’mimba, ankangomva thupi kuphwanya komanso amadwala malungo  pafupipafupi.  

Umboni woti Abiti ndi Gama amafuna Mgezenge akwatirenso Zikani  Pamene Mgezenge adadzamutula Nagama kunyumba kwawo, makolowa adamuuza Nagama  zinthu zotsatirazi:  

Munthu akaweta galu amayenera kumupatsa chakudya zonse chifukwa akapanda kutero  amagwira nkhuku za eni.  

Mlimi wang’ombe yamkaka amayenera kuyipatsa msipu ndi chakudya china choyenera ngati  akufuna izimupatsa mkaka wambiri ndipo ayenera kuonetsetsa kuti ng’ombeyo sikuchoka  m’khola.  

Akatswiri ankhondo amene amadumpha m’ndege yatombolombo; amene amadumpha ndi  chipangizo chokhala ngati chiambulera sangabwerere m’ndege adadumphamo kale.  Adamuuza Zikani kuti akufuna kuchita mwambo wa “Shazi” ndipo adamufotokozera  momveka bwino zifukwa zomwe iwo amafunira kuchita mwambowo.  

Zipangizo  

  1. Zifanifani  

Mukungoberekana ngati makoswe: Mukuberekana kwambiri  

  1. Zining’a  

Chiunda (kankhunda kakang’ono): Zikani  

Nkhunda yayikulu: Nagama, mkazi wa Mgezenge  

Akuthandize kusenza mtolo: Azigona ndi mamuna wako kuti aleke kudandaula  Mwamuna azingoyang’ana kudenga: Azingokhala osagona ndi mkazi wake.  Mgodi: Popezera ndalama ndi thandizo lina lofunikira  

Kuwedza chambo chonona kenako n’kuchitayira m’madzi momwemo: Kupeza mamuna  wachuma ndi kumusiyanso  

Sakulowa m’nyumba: Sakugona ndi mkazi wake monga banja.  

Kutaya bomwetamweta: Kutaya mamuna wopezapeza  

Zidzete: Zitsiru/Opusa/Opepera  

  1. Mikuluwiko  

Zengerezu adalinda kwawukwawu: Chidodo chimabweretsa mavuto. 

Munthu akaweta galu amayenera kumupatsa zakudya nthawi zonse chifukwa akapanda  kutero amagwira nkhuku za eni: Mgezenge, pamene adakwatira Nagama, anayenera  kupatsidwanso Zikani ngati Nagamayo samakwanitsa zinthu zoyenera mbanjamo poopetsa kuti  angatenge mkazi wadera osati m’bale wake wa Nagamayo.  

Mlimi wang’ombe yamkaka amayenera kuyipatsa msipu ndi chakudya china choyenera  ngati akufuna izimupatsa mkaka wambiri ndipo ayenera kuonetsetsa kuti ng’ombeyo  sikuchoka m’khola: Kuti Mgezenge apitirize kupereka ndalama zambiri kwa apongozi ake,  apongoziwo anayenera kumupatsanso Zikani ngati mkazi wabasera/wabanyira.  

Akatswiri ankhondo amene amadumpha m’ndege yatombolombo; amene amadumpha ndi  chipangizo chokhala ngati chiambulera sangabwerere m’ndege adadumphamo kale: 

Makolo a Zikani adachita chisankho chochita mwambo wa Shazi mwakuti sakadathanso  kubwerera m’mbuyo n’kusintha maganizo kamba ka maganizo a Zikaniyo.  

MAPHUNZIRO M’NUNSUYI  

  1. Mwano  

A gulupu adayankhula mwamwano kuti iwo sangakulitse dziko, pamene anthu  ankawadandaulira kuti asowa malo olima malingana ndi kubwera kwa msewu. 

2. Ndalama ikayankhula, chilungamo chimakhala chete.  

Mgezenge amapereka ndalama zambiri kwa apongozi ake ndipo patsiku limene adapita  ndi madandaulo ake nkukamusiya Nagama, adatenganso ndalama zambiri nawapatsa  amayi ake. Ndalama zimenezi zidachititsa kuti makolo asaganizire bwino mavuto omwe  mwana wawo amakumana nawo kubanja. Iwo adaganiza zopereka Zikani, mng’ono wake  wa Nagama kwa Mgezenge kuti akhale mkazi wake wachiwiri n’cholinga choti  azilandirabe ndalama.  

  1. Nkhanza  

Makolo a Zikani adamusiyitsa sukulu mtsikanayu kuti akwatiwe ndi mlamu wake  Mgezenge.  

Mayi a Nagama adamuuza kuti alibe mphamvu zowatsutsa pamene iwo ankamuuza za  ganizo loti Zikani alowe m’nyumba mwake ngati mkazi wachiwiri wa Mgezenge.  Mgezenge amafuna adzilowa m’nyumba ngakhale mkazi wake anali akudwala. 

4. Dyera  

Abiti adauza Nagama kuti sankafuna zoti Mgezenge akwatire kwina; akhalebe m’banja  lawo kuti ateteze chuma.  

  1. Ufulu 

Zikani adauza bambo ake kuti anali ndi ufulu wopitiriza maphunziro mwakuti atate  akewo sangamukakamize zokalowa m’nyumba mwa Mgezenge mlamu wake ngati mkazi  wake wachiwiri. 

  1. Kusamva maganizo a ena 

Makolo a Zikani sadafune kumva maganizo a mwana wawo pamene ankamupereka ngati  shazi kwa Mgezenge. Kuonjezera apo, a Gama adatsindika pomuuza Zikani kuti zimene  iwo alamula, alamula basi; palibe alandulepo. 

Matanthauzo amawu  

Mbirigha: Mkazi wabasera/wabanyira kwa mamuna pomuthokoza mamunayo kamba ka  mtima wake wabwino kapena wothandiza. 

error: Content is protected !!
Scroll to Top