MSCE Chichewa Galamala Form 3 and 4

AKAPANDAMNENI

Kapandamneni ndi gulu la mawu lomwe silikhala ndi mneni wosintha nthawi ndipo nthawi zina limagwira ntchito ngati mtundu wamawu.

Zitsanzo:

  • Tikupita ku Zomba.
  • Samakonda kudya mbatata.
  • Adabwera usiku zedi.
  • Ankatafuna ngati nkhumba.
  • Mwana wa abusa athu amatukwana zedi.

MITUNDU YA AKAPANDAMNENI

Kuti tidziwe mtundu wakapandamneni, tiyenera kuyeza mawu omwe ali paphata la kapandamneniyo.

  1. Wadzina: Amayamba ndi dzina ndipo amagwira ntchito ngati dzina.
  • Zitsanzo: Mwana osamvera malangizo amachititsa manyazi makolo.
  1. Wamfotokozi: Mawu apaphata pake ndi mfotokozi ndipo amagwira ntchito ngati mfotokozi.
  • Zitsanzo: Nkhuku yosayikira pakhomo imadyedwa ndi zilombo.
  1. Wamuonjezi: Amagwira ntchito ngati muonjezi, ngakhale kuti sinthawi zonse amayamba ndi muonjezi.
  • Zitsanzo: Amayenda ngati chitsiru.
  1. Wamperekezi: Ili ndi gulu lamawu lomwe limayamba ndi mperekezi.
  • Zitsanzo: M’chiuno mwa mwana simufa nkhuku.
  1. Wamfuwu: Amayamba ndi mfuwu ndipo amagwira ntchito ya mfuwu.
  • Zitsanzo: Kalanga ine! Ndavulala.
  1. Wamneni wosasintha nthawi: Mawu apaphata pake amakhala mneni wosasintha nthawi.
  • Zitsanzo: Ndidalephera kupita kusukulu.
error: Content is protected !!
Scroll to Top