MSCE Chichewa Literature Nthondo

Atengambali: Mayi ake a Nthondo, azimayi a m’mudzi, atsibweni ake a Nthondo, mlongo wake wa Nthondo, ndi ena ambiri.
Malo: Kumudzi kwawo kwa mayi ake a Nthondo

NKHANI YA M’MUTUWU MWACHIDULE

  • Nthondo adabadwa nthawi yozizira usiku.
  • Nthondo adali mwana yekhayo wamwamuna pomwe ena onse anali aakazi.
  • Anthu a m’mudziwo adapita kukayamikira kubadwa kwa mwana.
  • Nthondo anali mwana amene anayembekezeka kutsatira makolo ake polowa bulangete akakula.
  • Bambo ake a Nthondo anali atatengedwa ndi asilikali pamene iye anabadwa.
  • Uthenga wa kubadwa kwa Nthondo unatumizidwa kwa bambo ake a Nthondo.
  • A kwawo kwa bambo ake a Nthondo adalandira uthenga ndi chimwemwe chachikulu.
  • Amayi ake a bambo ake a Nthondo adakonzekera ulendo wokawona Nthondo.
  • Anthu a kwawo kwa bambo ake adayamikira kukongola kwa Nthondo ndipo adadziwitsidwa za kutengedwa kwa bambo ake ndi asilikali.
  • A kwawo kwa bambo ake a Nthondo adakhala kwa mayi ake a Nthondo kwa kanthawi.

MFUNDO ZIKULUZIKULU ZA M’MUTUWU

  1. Chisangalaro
  • Anthu a kumudzi kwa Nthondo adasangalala ndi kubadwa kwake.
  • A kwawo kwa bambo ake a Nthondo nawonso adakondwera ndi uthenga wa kubadwa kwa Nthondo.
  1. Miyambo
  • Bambo ake a Nthondo ankakhala chikamwini.
  • A kwawo kwa mayi ake a Nthondo adalengeza za kubadwa kwa Nthondo kwa akuchimuna.
  1. Kuthandizana
  • Anthu am’mudziwo adathandizana powafunira madzi mayi ake a Nthondo, popeza anali akadadwala.

MAPHUNZIRO AM’MUTUWU

  1. Ndibwino kuyamikira zinthu zabwino.
  2. Ndibwino kuthandiza anzathu pamene ali m’mavuto.

error: Content is protected !!
Scroll to Top