MSCE Chichewa Galamala Form 3 and 4

ANENI

  • Aneni ndi mawu amene amakamba za ntchito yochitika m’chiganizo komanso momwe chinthu chilili.

  • Aneni ena amaonetsa ntchito pamene ena saonetsa ntchito.

Zitsanzo:

  • (a) Dalitso wakumba dzenje lalitali. (mneni woonetsa ntchito)

  • (b) Mkango ndi chilombo cholusa. (mneni wosaonetsa ntchito)

MITUNDU YA ANENI

a. Woyambukira:

  • Amasonyeza yemwe wagwira ntchito komanso yemwe wachitidwa ntchito.

  • Aneniwa amanyamula zochitika kuchokera kwa mwininkhani kupita ku pamtherankhani.

  • Zitsanzo:

    • Kamba adapha bakha.

    • Amayi adya malalanje athu.

b. Wosayambukira:

  • Aneniwa sakhala ndi pamtherankhani, kotero kuti ntchito yake siyioneka kuti yachitika pa chinthu chilichonse.

  • Zitsanzo:

    • Fumulani wagwa lero.

    • Galu wafa.

c. Wodalira:

  • Amadalira mawu ena kuti apereke ganizo lomveka bwino.

  • Aneniwa alipo amitundu iwiri: amaphatikizo ndi amawu.

  • Zitsanzo:

    • Mandala ndi wabwino. (wamawu)

    • Hana anali ndi mwayi zedi. (“li” waphatikizo)

    • Akuti moni ambuyanu. (“ti” waphatikizo)

d. Wothandiza:

  • Amathandizira aneni ena poponga nthawi za aneni zosiyanasiyana.

  • Ntchitoyawo yeniyeni simaoneka, koma yomwe imaoneka ndi ya mneni wothandizidwayo.

  • Zitsanzo:

    • Nabanda wakhala akushashalika kwa zaka zambiri.

e. Wosintha nthawi:

  • Amasintha molingana ndi nthawi yakale, yatsopano, ngakhalenso yamtsogolo.

  • Zitsanzo:

    • Dimba adaphika maungu.

    • ANambewe ankaphika kale.

    • Mwana akuphika.

    • Mwayi adzaphika.

f. Wosasintha nthawi:

  • Awa sasintha molingana ndi nthawi ndipo amayamba ndi mphatikiram’mbuyo “ku”.

  • Zitsanzo:

    • Amakonda kupemphera.

    • Adazolowera kuyenda usiku.

    • Samatha kuphika.

    • Akufuna kukhala chitsiru.

MAGULU A ANENI

a. Mneni watsinde la phatikizo limodzi

  • Zitsanzo:

    • -ba, -psa, -swa, -fa, -mwa, -dya

    • Kagone waba nkhuku yanga.

    • Malinda wapsa ndi moto.

b. Mneni watsinde la maphatikizo awiri

  • Zitsanzo:

    • -lowa, -menya, -thyola, -zula

    • Talowa m’nyumba.

    • Adamenya mwana.

c. Mneni watsinde la maphatikizo atatu

  • Zitsanzo:

    • -khazika, -lalata, -lamula, -chepetsa

    • Khazikani mphika pamoto.

    • Tipita ndipo tikalalata.

d. Mneni wa tsinde la maphatikizo anayi kapena kuposera apo

  • Zitsanzo:

    • -piringiza, -changamutsa, -tsukuluza, -khulupirira

    • Amuchangamutsa anzake.

    • Ndimamukhulupirira Nambewe.

NTHAWI ZA ANENI

  • Izi zili ndi khalidwe la mneni poonetsa nthawi yomwe ntchito inachitikira, ikuchitikira, yachitikira ngakhalenso idzachitikira.

  • Nthawi za aneni zimapangidwa pogwiritsa ntchito aphatikiramkati osonyeza nthawi.

  • Zitsanzo:

    • Ankadya, timadya, tidzadya, tikudya.

MITUNDU YA NTHAWI ZA ANENI

  • Pali mitundu ikuluikulu itatu ya nthawi za aneni: nthawi yakale, yatsopano ndi yamtsogolo.

1. Nthawi yakale:

  • Yawamba:

    • Imakamba zinthu zomwe zinachitika ndipo zidatha.

    • Zitsanzo:

      • Ndidayamba uphunzitsi zaka zisanu zapitazo.

      • A Ngozo analedzera mowa kwambiri.

  • Yakawirikawiri:

    • Imasonyeza zinthu zomwe zimachitika kale kawirikawiri.

    • Zitsanzo:

      • Amadya zipokolo akadali ana.

      • Timatukwana tili kusekondale.

  • Yathayi:

    • Imasonyeza kuti pamene ncthito ina inkatha, ina idayamba kapena kuti pamene ntchito inkachitika inzake inali itatha.

    • Zitsanzo:

      • Ndidali nditakonzeka kale pamene ankanditenga.

      • M’mene ankawatema anali atadya kale.

  • Yopitirira:

    • Imasonyeza kuti ntchito inkachitika mopitirira kalero.

    • Zitsanzo:

      • Makolo athu ankavala nguwo.

      • Anali kudya usiku.

Kumbutso:

  • Nthawi yakale yopitirira imagwira ntchito izi:

    • i. kusonyeza chizolowezi komanso chikhulupiriro.

      • Zitsanzo:

        • Makolo ankayenda pangolo.

        • Anthu akale anali kupembedza mizimu.

    • ii. kusonyeza kuti ntchito inali kupitirira pamene inzake imachitika.

      • Zitsanzo:

        • Mphatso anali kuodzera ife tikupemphera.

        • Gandali ankadya iwo akuphunzira.

  • Yathayi yopitirira:

    • Imasonyeza kuti ntchito inkachitika m’mbuyomo mopitirira kufikira nthawi ina yake.

    • Zitsanzo:

      • Tidakhala tikudya mtoliro kwa sabata yathunthu.

      • Adakhala akutipondereza kwa zaka zisanu.

2. Nthawi yatsopano:

  • Imasonyeza zinthu zimene zikuchitika kapena zangochitika kumene.

  • Yawamba:

    • Imagwiritsa ntchito mphatikiramkati “-ma-”.

    • Zitsanzo:

      • Timadya zipokolo.

      • Angoni samasankha ndiwo.

  • Nthawi yatsopano yawamba imagwira ntchito zotsatirazi:

    • i. kusonyeza chizolowezi.

      • Zitsanzo:

        • Solobala amaseka mopusa.

        • Thokozani amayankhula mokuluwika.

    • ii. kusonyeza zikhulupiriro.

      • Zitsanzo:

        • Akhirisitu amakhulupirira Yesu.

        • Satana amamwa mwazi.

  • Yathayi:

    • Imasonyeza kuti ntchito yangotha kumene koma zotsatira zake zikadalipo.

    • Zitsanzo:

      • Tamenya nkhondo yabwino.

      • Ndalima ndime yayikulu.

  • Yopitirira:

    • Imasonyeza kuti ntchito ikuchika mopitirira.

    • Zitsanzo:

      • Ali kusonyeza zomwe akolola.

      • Ife tikusamba.

  • Yathayi yopitirira:

    • Imasonyeza kupitirira kwa ntchito ndi kutha kwa nthawi yonenedwayo.

    • Zitsanzo:

      • Takhala tikulandira malipiro ochepa kwa zambiri.

      • Wakhala akudwala kwa nthawi yayitali.

      • Anthuwa akhala ali kukupirirani.

3. Nthawi yamtsogolo:

  • Imakamba za ntchito zomwe zidzachitika mtsogolo.

  • Yawamba:

    • Imagwiritsa ntchito mphatikiramkati “-dza-”.

    • Zitsanzo:

      • Udzadya thukuta lako.

      • Tidzapuma sabata yamawa.

  • Yathayi:

    • Imaonetsa ntchito yomwe idzachitike mtsogolo itatha.

    • Zitsanzo:

      • Udzakhala utalambula bwaloli pofika pa 23 August 2010.

      • Tidzakhala titayala nkhata pokwirira dzenjelo.

  • Yopitirira:

    • Aneni ake amasonyeza kuti ntchito izidzachitika mopitirira kutsogolo.

    • Zitsanzo:

      • Nkhondo zidzachitika kwa masabata atatu.

      • Mafilimu adzachitika pa intaneti masiku angapo.

MAGULU A NTHAWI ZA ANENI

a. Mphatikiridwa

  • Pali mitundu iwiri:

    • Poyamba, akufotokozera mawu otero monga “ali” ndi “kudzalu.”

    • Pothandizidwa ndi mphatikiridwa.

b. Zinthu

  • Mofanana ndi mphatikiridwa, zinthu zimagawidwa mu zitsanzo ziwiri:

    • Zinthu zomwe zili ndi mphamvu yotsogolera, monga, “ndidayamba.”

    • Zinthu zopanda mphamvu, monga, “ndidya” yomwe ikukwaniritsidwa kuchokera m’nthawi yapitayi.

Zitsanzo Zopeza Aneni:

  1. Aneni amasonyeza njira ziwiri kapena zingapo zovuta popanda mawu.

  2. Malemba akuzungulira aneni akhala akuchitika ndi anthu asanayambe.

  3. Ndiyenera kutchula akale, nthawi ya lero, komanso zinthu zatsopano.

MAFUNSO AKE

  1. Kodi aneni anenetsa chiyani?

  2. Ndizofunika bwanji kuti aneni akhalebe ndi zotsatira za malinga ndi nthawi?

  3. Chifukwa chiyani ndi bwino kusonyeza mawu akale pofuna kutsatira aneni?

ZOFUNA KUYAMBA:

  • Onetsetsani kuti aneni akuchita zinthu zolemera, zambiri, komanso zolondola.

  • Kapenanso bwanji chindapusa chiyamba kukhala chapamwamba chomwe chingathandize kusonyeza aneni a m’mbuyomu?

 

KACHITIDWE KA ANENI

Ili ndi khalidwe lamneni losonyeza mgwirizano pakati pa mwininkhani, pamtherankhani ndi mneniyo.

MITUNDU YA KACHITIDWE KA ANENI

  1. Kachitidwe kawochita: Mwininkhani amayamba chiganizo ndipo chidwi cha woyankhula chimakhala pa yemwe wachita ntchito m’chiganizo.

  • Zitsanzo:

    • Galu wanu waponda chimanga changa.

    • Mbuzi zabudula bonongwe.

  1. Kachitidwe kawochitidwa: Pamtherankhani amayamba chiganizo kusonyeza kuti ntchito yamuchitikira ndipo chidwi cha woyankhula chimakhala pa yemwe wachitidwa ntchito.

  • Zitsanzo:

    • Chimanga changa chapondedwa ndi galu wanu.

    • Bonongwe wabudulidwa ndi mbuzi.

Kachitidwe Kawochitidwa Kali Ndi Mitundu Yake:

  1. Kawochitidwa poyera: Aneni ake amathera ndi mphatikiramtsogolo “-idwa-” ndi “-edwa-”

  • Zitsanzo:

    • Ana alasidwa ndi zigawenga.

    • Nkhumba yabedwa dzulo.

  1. Kawochitidwa m’chibisira: Aneni ake amathera ndi mphatikiramtsogolo “-ika-” komanso “-eka-”

  • Zitsanzo:

    • Nsima yadyeka.

    • Mtolo wamangika bwino.

III. Kawochitidwa monyazitsa: Aneni ake amathera ndi mphatikiramtsogolo “-iwa-”, “-ewa-” ndi “-wa-”.

  • Zitsanzo:

    • Galu waphewa.

    • Kamoto watengwa.

    • Ndipsi yamangwa.

    • Joza wapezwa ndi mkazi uja.

MISINTHO YA ANENI

Msintho wamneni ndi kusintha komwe kumachitika pamneni pamene tayika mphatikiramtsogolo wosinthira mneniyo.

Msintho wamneni

Mtundu wa msintho wamneni

Mphatikiramtsogolo

matidwa

Wochitidwa poyera

-idwa, -edwa

matika

Wochitidwa m’chibisira

-ika, -eka

matiwana

Wochitidwa monyazitsa

-iwa, -ewa, -wa

matamata

Wachibwereza

matula

Wamtsutso/wotsutsa

-ula

matana

Wochitirana

-ana

mobwezerana

Womchitira

matira

   

matitsa

   

matitsitsa

Wochititsa

-ira, -era

 

Wokitzitsa

-itsa, -etsa

 

Wochititsitsa

-itsitsa, -etsetsa

KANENEDWE KA ANENI

Iyi ndi ntchito yomwe aneni amagwira m’chiganizo molingana ndi m’mene akumvekera, monga: kufotokoza, kufunsa, kulamula, kusonyeza cholinga ndi zina.

MITUNDU YA KANENEDWE KA ANENI

  1. Kofotokoza: Aneni ake amangouza anthu (amangofotokoza) zomwe zachitika kuti adziwe chabe.

  • Zitsanzo:

    • Mvula imagwa yochepa kuchipalamba.

    • Masika sadayende bwino.

  1. Kofunsa: Kawirikawiri aneni ake amatchulidwa mofunsa koma satsatana ndi mawu ofunsira monga: “kodi”, “bwanji” ndi ena.

  • Zitsanzo:

    • Mwadya kale?

    • KuMalawi mumafunsira amuna?

  1. Kolamula: Aneni amkanenedweka amapereka lamulo ndipo kanenedweka kalipo kamitundu itatu:

  • Kolamula wamba/mwachindunji: Aneni ake amapangidwa ndi tsinde lamneni kapenanso tsinde ndi mphatikiramtsogolo wolemekeza kapena kuchulukitsa (“-ni”)

    • Zitsanzo:

      • Pita uko.

      • Pitani uko.

      • Yala apa.

      • Yalani apa.

  • Kolamula mopempha/molangiza:

    • Zitsanzo:

      • Baalemba nthawi siyinathe.

      • Kathamanga sunamalize.

  • Kolamula mokakamiza: Lamulo limagwa kwa aliyense wonyozera ntchito yomwe wauzidwa. Aneni ake amakhala ndi mphatikiramkati “-zi-”.

    • Zitsanzo:

      • Kazilemba mwachangu.

      • Kazilimani ndingakuthamangitseni.

  1. Kachifuniro: Kamasonyeza kuti zoyankhulazo ndi maganizo a woyankhulayo osati ndi choncho nthawi zonse. Kanenedweka kamasonyeza izi:

  • Kupempha chilolezo (kanenedwe kopempha chilolezo)

    • Zitsanzo:

      • Ndingapite nawo ku Zomba lero?

      • Timati titenge nawo mwanayu.

  • Kusonyeza mafuno (kanenedwe ka mafuno):

    • Zitsanzo:

      • Muuse mumtendere.

      • Uziona kutali ndi moto.

      • Mulembe bwino mayeso anu.

  • Kusonyeza kutheka kwa chinthu (kanenedwe kosonyeza kutheka ndi kusatheka kwa ntchito):

    • Zitsanzo:

      • Ndingawuluke patsache.

      • Uyu angapapire bibida.

      • Iwe wekha sungandimenye.

      • Sangasenze mtolo wankhuni.

  • Kusonyeza cholinga (kanenedwe kacholinga): Aneni ake amasonyeza kuti ntchito yachitika ndi cholinga chake.

    • Zitsanzo:

      • Adavina mosangalatsa kuti alandire mphatso.

      • Tidakhamukira ku malo ogona kuti tikapulumutse mabuku athu.

      • Adamulemba pamsana kuti asadzamuyiwale.

  1. Kapokhapokha: Aneni ake amapereka muyeso wachinachake kuti ufikitsidwe ndipo amasonyeza kuti ntchito ichitika inzake ikakwaniritsidwa. Aneni akakhala ndi mphatikiramkati wapokhapokha “-ka-”.

  • Zitsanzo:

    • Mukasankha Kamanuyu tidzavutika zedi.

    • Mukadafuna mukadalenga galu.

    • Mukadandipempha chilichonse ndikadakupatsani.

  1. Kazotsatira: Aneni ake amasonyeza kuti ntchito idachitika/idakwanitsidwa motsatiridwa ndi inzake (ntchito itachitika, inzake idatsatira).

  • Zitsanzo:

    • Atawerenga kwambiri adapambana mayeso.

    • Ndidalira kwambiri mwakuti ndidatupa maso.

    • Atamuchotsa sukulu adadzimangirira.

error: Content is protected !!
Scroll to Top