MSCE Chichewa Galamala Form 3 and 4

APEREKEZI

Awa ndi mawu amene amaperekeza dzina kapena mlowam’malo. Zitsanzo:

  • Bwerani kwa ine nonse olemba ndi ovutika.
  • Ndagula fanta chifukwa cha iwe.

MAGULU A APEREKEZI

  1. Mperekezi wamawu amodzi
    Zitsanzo:
  • Tikupita ku Nsaka.
  • Wakhala pa chitsa.
  • Ndidzakumenya ndi ichi.
  1. Mperekezi wamawu awiri
    Zitsanzo:
  • Mukabisale pansi pa bedi.
  • Tidampeza kuseri kwa chigayo.
  • Tinkayenda mphepete mwa msewu.
  • Wamwalira kamba ka malungo.

NTCHITO ZA APEREKEZI

  1. Kusonyeza chipangizo/chida
    Zitsanzo:
  • Adamukwapula ndi tsatsa.
  • Ndikugwaza ndi chisongole.
  • Adabwera pa galimoto.
  • Tinkauluka pa tsache.
  1. Kusonyeza mbali yomwe chinthu chili (malo)
    Zitsanzo:
  • Mwana wapita ku Matawale.
  • Atate ali pa phiri.
  • Akuyenda pakati pa msewu.
  • Ndidamuona m’mbali mwa khola.
  1. Kusonyeza umwini
    Zitsanzo:
  • Musadye mapapaya a Nagwede.
  • Ng’ombe izi ndi za amalume.
  1. Kusonyeza nthawi
    Zitsanzo:
  • Tilemba mayeso mkati mwa Juni.
  • Kodi udabadwa pakati pa mwezi?
  • Ndidzapitako pa chisanu.
  1. Kusonyeza kuchita ntchito ndi wina kapena chinthu china
    Zitsanzo:
  • Mukadya ndi alendo.
  • Apita ndi atsibweni.
  • Ndayenda ndi ndalama.
  • Mugule ndi ndalama zanu.
  1. Kusonyeza chifukwa
    Zitsanzo:
  • Mwabwera kuno kumudzi chifukwa cha matendawa.
  • Mwanayu afa kamba ka uhule.
  • Kodi mwagulitsa Malaya chifukwa cha mtsikanayu?
error: Content is protected !!
Scroll to Top