MSCE Chichewa Literature Nthondo

Malo

  • Kwawo kwa Nthondo, kwa mfumu yaikulu

Atengambali

  • Nthondo

  • A Dzeya

  • A Chembe

  • A Mzingwa

  • Anthu am’mudzi

  • Anthu a kwa mfumu yaikulu

NKHANI YA M’MUTUWU MWACHIDULE

  • Atsibweni a Nthondo anadwala, ndipo Nthondo anatumidwa kukanena uthenga kwa mfumu yaikulu, koma asanapite, atsibweni akewo anamwalira.

  • Nthondo anatumidwa kukanena uthenga wa malirowo kuchokera kwa mfumu yayikulu, adapeza malirowo ataika kale.

  • Anthu am’mudzimo atasonkhanitsana, akazi (mbumba) adasankha Nthondo kukhala woyenera ufumu.

  • Anaphika mowa ndi kutumiza uthenga kwa mfumu yayikulu kuti adzakhale nawo pa mwambowo.

  • Patapita masiku angapo, mwambowo unachitika, ndipo Nthondo analowa ufumu, anampatsa malangizo osungira mudzi, ndipo anthu onse anamwazikana.

  • A Mzingwa ndi a Dzeya adafuna kumuwuza Nthondo kuti asathetse Mzinda chifukwa choti iyeyo ndi Mkhristu, podabwa kuti maliro akamachitika m’mudzimo, Nthondo samachita Mzinda.

  • Nthondo anakana maganizo a nduna zija, ndipo anaziuza kuti amene sankafuna sukulu achoke m’mudzimo.

  • A Dzeya ndi a Mzingwa anamuyesa Nthondo ngati wachibwana, ndipo anachoka pamalopo mokwiya.

  • Nthondo analimbikitsa anthu am’mudzimo kupita ku sukulu pamodzi ndi ana ake omwe ankawakalipira akajomba kusukulu.

  • Anthu ambiri adayamba kupeza phindu mu sukulu, ndipo ambiri amasandulika a Khristu chifukwa chodziwa za chikondi cha Ambuye Yesu.

  • Nthondo adakhalabe mfumu kwa zaka zingapo, ndipo anjala amawathandiza ndi kuwapatsa chakudya, ndinso otetana (amikangano, ofooka) adawaletsa ndi kuwakhazika mu mtendere.

  • Tsiku lina, Nthondo anadwala chibayo (chilaso), ndipo anthu ambiri anabwera ndi mankhwala awo, koma analephera Nthondo ndi kumwalira.

  • Anthu ambiri anamva chisoni ndi maliro a Nthondo chifukwa cha ntchito zake zabwino.

  • M’phunzitsi adatsiriza ndi pemphero pa mwambo wa malirowo, ndipo anthu ambiri adamuyesa Nthondo ngati mtsogoleri amene adawatengera chokoma m’mudzi mwawo.

MFUNDO ZIKULUZIKULU ZA M’MUTUWU

a. Kudalira

  • A kwawo kwa Nthondo anadalira anthu a kwa mfumu yaikulu pa maliro a atsibweni ake a Nthondo.

  • Anthu am’mudzi anadalira akazi kuti asankhe munthu woyenera kukhala mfumu.

  • Anthu am’mudzi anadalira anthu a kwa Mfumu yaikulu pa mwambo wolonga Nthondo ufumu.

  • A Dzeya ndi a Mzingwa anadalira Nthondo kuti asathetse Mzinda m’mudzimo.

  • Nduna zinadalira Nthondo kukanena uthenga wa maliro kwa mfumu yaikulu.

b. Kudalirana

  • A Dzeya ndi a Mzingwa anadalirana pokamuwuza Nthondo kuti asathetse Mzinda.

c. Miyambo

  • Mwambo wa maliro a atsibweni ake a Nthondo ndinso wa maliro a Nthondo.

  • Mwambo wolonga ufumu Nthondo.

d. Chisoni

  • Anthu anali ndi chisoni pa maliro a atsibweni ake a Nthondo.

  • Anthu anali ndi chisoni pa maliro a Nthondo.

e. Udindo ndi Kuthandiza

  • Nthondo ankathandiza anthu anjala pamene iye adali mfumu.

  • Nthondo ankathandiza anthu otetana.

  • Nthondo ankalimbikitsa anthu kupita ku sukulu.

f. Kudzidalira

  • Nthondo anadzidalira yekha poyankha nduna kuti amene ankafuna mzinda achoke pamudzipo.

g. Malangizo

  • Nthondo adamulangiza za kasungidwe ka mudzi pamene ankamulonga ufumu.

h. Kuthandizana

  • Anthu am’mudzi anathandizana pa matenda ndi maliro a atsibweni ake a Nthondo.

  • Anthu am’mudzi anathandizana pa matenda ndi maliro a Nthondo.

i. Ukhrisitu

  • Anthu ambiri amaphunzira sukulu ndi kusandulika a Khristu.

error: Content is protected !!
Scroll to Top